Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 49

Sewero la Mfumu Edipa n’choti nonse simunabisike kwa ine. Ndikutha kukuzindikirani ngakhale sindikutha kukuwonani. WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Inuyo mwakumana ndi zinthu zochititsa mantha kwambiri, ndiye n’chifukwa chiyani mwadziwonje- zeranso mavuto ena podzibowola maso? Ndi mulungu uti amene waku- limbikitsani kuchita zimenezi? EDIPA: Ndi Apolo mbale wanga. Apolo ndi amene wandibweretsera tsoka limeneli. Koma ponena za masowa ndiye sindingamunamizire. Masowa ndawachotsa ndi manja angawa. Ndikuwona kuti palibenso chifukwa chokhalira ndi maso ndi moyo wanga womvetsa chisoniwu. Chilichonsetu chomwe ndingawone sichingandibweretsere chimwe- mwe? WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Zimene wanenazo ndi zowona zokhazokha. EDIPA: Ndi chiyani chimene ndinganene kuti ndingalakelakenso kuchi- wona? Ndi ndani amene angandipatse moni ine n’kusangalala? Chonde abale anga, ndichotseni kuno. Ndipirikitseni mumzinda muno. Milungu yandipatsa chilango chopweteka kwambiri itandiwona kuti ndine wopa- nda phindu. WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Zikuwonekeratu kuti mulibiretu mtendere wam’maganizo. Ngakhale ineyo ndikanakonda ndikanapanda kukudziwani, ndipo ndikuganizanso kuti zikanakhala bwino mukana- panda kubadwa. EDIPA: Munthu amene anandipulumutsa n’kundimasula miyendo kuti ndisafe ndi wotemberedwa kwambiri. Chifundo chimene anandichitira si chabwino ngakhale pang’ono. WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Mukunenazo ndi zowona zokha- zokha. Nanenso ndikanakonda mukanangofa kale lomwelo. Koma na- nga titani popeza zinachitika kale! EDIPA: Mwinadi zikanatero sindikanapha bambo anga ndipo anthu sakanandiwona ndikukwatira mayi anga ondibereka. Tsopano onani milungu yandinyanyala. Ndingakhalenso bwanji ndi mtendere wam’ma- 44