Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 50

Sewero la Mfumu Edipa ganizo pamenepo? Ngati pali mavuto owopsa kwambiri amene anthu amakumana nawo, ndiye ineyo ndawawona ndi kuwagwira komwe. WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Koma ine sindikuwona kuti mwachita zanzeru podzibowola masowo. Kodi simudziwa kuti ndi bwino kumwalira kusiyana ndi kukhala wosawona? EDIPA: Usandiwuze kuti zimene ndachitazi si zabwino. Ndipo kungo- chokera pano sindikufunanso kumva zonena zako. Ukuganiza kuti ndi- kanakhala kuti ndadzipha ndikanakakumana bwanji ndi bambo koma- nso mayi anga ku Hade? Anthu awiri amenewa ndinawachitira zonya- nsa zazikulu kwambiri moti ngakhale nditadzipha sizingakhale zokwa- nira kufafaniza machimo anga. Mwina ukuganiza kuti kuwona ana anga kungandipatseko chimwemwe, koma ayi ndithu. Tangowona mmene anabadwira! Sindingasangalale n’komwe kuwona nkhope zawo. Sindi- ngasangalalenso kuwona mzindawu limodzi ndi makoma ake. Mtendere sindingawupeze kuwona zithunzi zopatulika za milungu yathu. Ndine munthu wotembereredwa kwambiri. Ineyo ndakhala ndikunena kuti ndidzathamangitsa munthu aliyense amene atapezeke ndi mlandu ume- newu ndipo ndikanachita zimenezi mopanda chisoni. Ndiye tawonani matemberero onse aja agwera pamutu panga. Ndine ndani kuti ndize- mbe chilango chimenechi. Ndine chodetsa chonyansa kwambiri mumzi- nda muno. Sindikuwona kuti chikanakhala chanzeru kukhalabe ndi maso n’kumawona nkhope zanu. Ndipo zikanakhala kuti n’zotheka kuti ndichonse chimene chimandichititsa kuti ndizimva, n’kanachizula ndi mitsitsi yomwe kuti ndisamvenso zonena za aliyense. Ndikuganiza kuti munthu angapezeko kamtendere ngati atakhala yekha, osamva kapena kuwona zimene zikuchitika m’dzikoli. Oo, Thebesi, n’chifukwa chiyani unandilola kuti ndipezeke kuno? N’chifukwa chiyani sunandiwononge kapena kundibweza pamene ndinkabwera kwa iwe kuti ndisadzawu- lulire anthu zokhudza mmene ndinabadwira? Aa, a Polebasi komanso mzinda wa Korinto, dziko limene anthu ankanena kuti ndiye kwathu. Munandilera bwino kwambiri moti anthu ankandisirira. Chonsecho ndinali wodetsedwa kuyambira m’mimba. Tsopano aliyense wadziwa kuti ndine chinthu chonyansa, munthu yemwe ndi wotembereredwa kuyambira pakubadwa kwanga. Iwe malo omwe panakumana misewu 45