Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 48

Sewero la Mfumu Edipa NTHENGA WACHIWIRI: Kayatu! Akungowuza aliyense kuti akufuna akumane ndi anthu onse kuti awalongosolere zoti ndi iwowo amene anapha bambo awo komanso kukwatira . . . mwina ndisabwerezenso mawu amenewa chifukwa ndi owumitsa pakamwa kwambiri. Akuti akufuna kuti anthu awapirikitse mumzinda muno kuti tsoka limene ali nalo lisakhudze tonsefe. Koma afowoka kwambiri moti akufunikira mu- nthu woti aziwachirikiza. Zikuwoneka kuti akumva ululu woposa nsi- nkhu wawo. Posachedwapa muwawona zipatazi zikangotsegulidwa. Muwona zinthu zomwe simunayambe mwaziwonapo ndipo sindikuka- yikira kuti chisoni chikugwirani. [EDIPA akutuluka m'nyumba yachifumu.] WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Koma chaka chino tiwona malo- dza ndithu. Munthu womvetsa chisoni iwe, kodi wachita misala kuti ufike podzipweteka chonchi? Kodi unayambana chiyani ndi milungu kuti ikuwononge chonchi? Ngakhale kuti pepa sapoletsa chilonda, ndi- kufuna ndikupepese chifukwa cha mavuto akugwerawa. Kunena zowo- na wandimvetsa chisoni moti ndangokhala wodzigwira chifukwa ndika- nakhala wina ndikanagwetsa misozi. Ndili ndi mafunso ambirimbiri omwe ndikufuna kukufunsa koma pakamwa pangondiwuma! EDIPA: Ndine munthu womvetsa chisoni kwambiri, munthu wotembe- reredwa. Zikanakhala bwino ndikanapanda kuliwona dzikoli. Nanga ndilowera kuti ine? WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Ulowera kudziko lomwe anthu amathawako, dziko lomwe anthu salifuna. EDIPA: Mdima wandikuta chifukwa cha munthu wosadziwika yemwe anabwera pano ndi chowonadi chosatsutsika. Zikungokhala ngati lu- panga lakuthwa landilasa mumtima. Sindikufunanso kukumbukira kale langa ngakhale pang’ono. WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Koma ndiyetu wakumana nazo m’bale wanga. Ukungokhala ngati walangidwa kawiri. EDIPA: Abale anga, zowona mudakasamala za ine? Sindimaganizira kuti mungapitirizebe kundichitira chifundo ndi kusawona kwangaku. Pepani kwambiri chifukwa cha machimo angawa. Chikundiwawa 43