Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 47

Sewero la Mfumu Edipa mwana yemwe anabereka zaka zambiri zapitazo, mwana amene ulosi unanena kuti adzapha bambo ake n’kukwatira mayi ake. Iye anagona pakama akulira, pakama yemwe ankagona limodzi ndi Layasi. Kenako anabereka mwana yemwe anadzakhala mwamuna wake n’kumubereke- ranso ana. Tikakamba za mmene anafera ndiye sindikudziwa kuti zina- khala bwanji. Kenako tinangowona a Edipa atulukira. Ife timangowaya- ng’ana akuyenda molowera uku ndi uku akudziguguda pachifuwa. Pa- mene amachita zimenezi amatipempha kuti tiwapatse lupanga. Nawo- nso anali ndi chisoni chachikulu pozindikira kuti anakwatirana ndi mayi awo. Kenako anangokhala ngati agwidwa ndi chiwanda, moti palibe munthu amene analimba mtima kuwayandikira. Anakuwa kwambiri n’kuthamanga kukamenya chitseko chachipinda chomwe Yokasi ana- dzikhomera ndi phewa lawo moti chokhomera chake chinatotokoka. Atangolowa anawona Yokasi ali lendelende m’mwamba, atadzimangi- rira. A Edipa atangowona malodzawo, anayamba kulira mowawidwa mtima ndipo anachotsa thupi la Yokasi pachingwecho n’kuligoneka pa- nsi. Zimene zinachitika pambuyo pa zimenezi zinali zoziziritsa thupi. Tinangowona a Edipa akuthothola kachitsulo kena pachovala cha Yokasi ndipo anakweza dzanja lawo m’mwamba n’kuzika chitsulocho m’maso mwawo. Pamene amachita zimenezi amafuwula kowopsa kuti: “Suku- yenera kudzawonanso zinthu zonse zowopsa zimene wawona, kapena kudzachitanso zinthu zochititsa mantha zimene wachita! Wawona zi- nthu zambiri zimene sumayenera kuwona. Choncho kuyambira lero mpaka m’tsogolo uzingowona mdima wokhawokha.” Amanena mawu amenewa akubowola maso awowo ndi chitsulocho. Amati akachizika, magazi amatuluka mowopsa kuchokera m’maso mwawo n’kumayende- rera mpaka kundevu. Magaziwo samatuluka pang’onopang’ono, ama- ngokhala ngati mtsinje wodzadza ndi madzi m’nyengo yadzinja. Zimene achita zatiwopsa kwambiri. Tsoka lochititsa mantha lawomba munthu ndi mkazi wake ngati mphenzi. Chisangalalo chonse chimene anali na- cho chasanduka chisoni, moti pano kwatsala n’kulira komanso mavuto okhawokha. Zikungokhala ngati mavuto onse omwe amagwera anthu angowakhuthukira nthawi imodzi. WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Ndiye iwowo amaganiza kuti kudzivulazako kuwachepetsera ululu womwe akumva mumtima? 42