Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 46

Sewero la Mfumu Edipa EDIPA: Ngati zimenezo zinali zowona, n’chifukwa chiyani munamupe- reka kwa munthu wachikulireyu m’malo mongomupha? WANTCHITO: Ankandimvetsa chisoni. Ndiye nditamva zoti mnzanga- yo amachokera kudziko lina, ndinawona kuti ndingomupatsa kuti aka- fere kumeneko m’malo moti ndimuphe ndi manja anga. Ndinkawona kuti sangapulumuke chifukwa anali atavulala kwambiri. Zikuwoneka kuti mnzangayo anamupulumutsa, koma sankadziwa kuti akusungira kanjinji, yemwe anali kudzatukusira m’tsogolo. Musangalala kudziwa kuti mwana amene tikunenayu ndi inuyo. Kubadwa kwanu linali the- mberero lalikulu. EDIPA: Kalanga ine, kuteroko ulosi uja unakwaniritsidwa! Oo, kuwala, ndilole kuti ndikuwone komaliza. Ine ndi munthu wotembereredwa kuyambira ndili m’mimba mwa mayi anga. Nalonso banja lomwe ndina- badwira ndi lotembereredwa kwambiri. Chinandiwona n’chiyani kuti ndiphe munthu yemwe sindinkayenera kumupha? [EDIPA akulowa m'nyumba yachifumu. Patapita nthawi, NTHENGA WA- CHIWIRI akutuluka kuchokera m'nyumbayo.] NTHENGA WACHIWIRI: Pepani kwambiri akuluakulu, zomwe zachi- tika m’nyumbamu sindizo. Ndikuganiza kuti palibe mtsinje womwe ungatsuke nyansi komanso zinthu zochititsa nseru zomwe nyumbayi yakhala ikubisa. Posachedwapa itiwonetsa zosawona. Zimene Yokasi ndi a Edipa achita m’nyumbamu ndi zowopsa kwambiri. WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Bwanjinso? Zowopsatu zomwe tangomva posachedwapa zatiwiritsa kale mitu. Ukufunanso kutiwuza chiyani chomwe chingakhale chowopsa kuposa pamenepo. NTHENGA WACHIWIRI: Mfumukazi Yokasi yadzipha! WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Wati chiyani? Zinakhala bwanji? NTHENGA WACHIWIRI: Muli ndi mwayi kuti simunawone zimene zachitika. Zinali zowonekeratu kuti Yokasi amavutika mumtima pamene amalowa m’nyumbamu. Wayenda chothamanga mpaka kukalowa ku- chipinda chake. Atangolowa, anakhoma chitseko ndipo anayamba kuli- rira Mfumu Layasi, yomwe inamwalira kalekale. Iye anakumbukira 41