Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 45

Sewero la Mfumu Edipa chitike ndikakuwuzani chilungamo. EDIPA: Akuluakulu, munthuyu ndi wosamva. Mugwireni ntchito! WANTCHITO: Tayimani kaye! Komatu ndakuyankhani funso limene munandifunsa! Ndanena kuti ndinedi amene ndinamupatsa mwanayo. EDIPA: Chabwino, ndiye munamutenga kuti mwanayo? Munamutenga kunyumba kwanu kapena kwinakwake? WANTCHITO: Sanali wanga, munthu wina ndi amene anandipatsira. EDIPA: Munthu wake ndani? Anali wa mumzinda muno kapena ayi? Nanga dzina lake ndi ndani? WANTCHITO: Chonde mbuyanga musapitirize kundifunsa mafunso amenewa! Ndikhululukireni chifukwa sindikwanitsa kuwayankha. EDIPA: Mukufuna muziyankha mukulira? WANTCHITO: Ayi, basi ndifotokoza. Mwanayo anabadwira m’nyumba ya Mfumu Layasi. EDIPA: Anali mwana wa kapolo wake kapena wa wachibale wake? WANTCHITO: Ndisanameyi, mafunso amene mukundifunsawa akundi- sowetsa chonena . . . N’zowumitsa pakamwatu! EDIPA: Kaya n’zowumitsa pakamwa, ndiwuzeni. Ndikufunika kudziwa chilungamo. WANTCHITO: Popeza mwandikakamiza, ndikuwuzani. Anandiwuza kuti mwanayo anali wake. Ndikuganiza kuti mkazi wanu ndi amene angakuwuzeni zambiri zokhudza nkhani imeneyi. EDIPA: Mukutanthawuza kuti iwowo ndi amene anakupatsani mwana- yo? WANTCHITO: Inde. Anandiwuza kuti ndikamuphe. EDIPA: Mayi a mwanayo anali ndani? Yokasi? WANTCHITO: Inde. Zikuwoneka kuti ankawopa ulosi wina wowopsa womwe analandira kuchokera kwa Apolo. EDIPA: Ulosi wake wotani? WANTCHITO: Ulosi wakuti mwanayo adzapha bambo ake. 40