Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 44

Sewero la Mfumu Edipa imeneyo ngati mukuyikumbukira kale? Mukufuna kundipala mkamwa? NTHENGA: Ayi. Ndimangofuna kukuwuzani kuti munthu wayima apayu, ndi mwana amene unandipatsa uja. WANTCHITO: Choka apa! Bwanji osaphunzira kukhala chete pa nkhani zomwe sizikukukhudza? EDIPA: Bambo, takhalani kaye chete! Musayambe kumunyoza mnza- nuyu. Zimene inuyo mwanena ndi zimene zili zokayikitsa kwambiri ndikayerekezera ndi zimene mnzanuyu wanena. WANTCHITO: N’chifukwa chiyani mwandipsera mtima? Pali chimene ndakulakwirani? EDIPA: Sunandiwuze zokhudza mwana amene unamupereka kwa munthuyu. WANTCHITO: Zimenezotu ndi zimene munthuyu wakuwuzani! Nanga ndi ine ngati? Ngati wayiyamba nkhaniyi akufunikanso kuyimalizitsa. EDIPA: Ngati mutapandatu kutiwuza zowona zenizeni mwamtendere, dziwani kuti munena zimenezi mukumva ululu wowopsa. Tikukhawu- litsani. WANTCHITO: Chonde mbuyanga, musazunze munthu wachikulire! EDIPA: Asilikali, tamumangani munthuyu asatitayitse nthawi! WANTCHITO: N’chifukwa chiyani mukuchita zimenezi? Mukufuna ndikuwuzeni chiyani? EDIPA: Ndakuwuza kaletu paja. Ndikufuna kudziwa zokhudza mwana amene munamupereka kwa munthuyu. N’zowona kuti munachitadi zimenezi? WANTCHITO: Inde, ndipo ndikanakonda ndikanangofa m’mbuyo momwemo. EDIPA: Mwina ndikuwuzeni kuwopsa kwa zimene zingachitike ngati mutandiwuza zabodza. Ndiwuza asilikaliwa kuti akupaneni, mukapa- ndabe kuwulula ndiwawuza kuti azikudulani chiwalo chimodzichimo- dzi mpaka thupi lanulo lithe! WANTCHITO: Ndikuganiza kuti sizikhala zosiyana ndi zimene zinga- 39