Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 43

Sewero la Mfumu Edipa Mfumu Layasi? WANTCHITO: Mwalasa ndithu. Koma sikuti ndinali kapolo, kungoti ndinakulira m’nyumba mwake. EDIPA: Nanga unkagwira ntchito yanji? WANTCHITO: Ndinkagwira ntchito yoweta nkhosa. EDIPA: Unkaziwetera kuti? WANTCHITO: Kumapiri a Katero komanso madera ena ozungulira kumeneko. EDIPA: Unayamba wakumanapo ndi munthu uyu pamene unkaweta nkhosa za mbuye wako kumeneko? WANTCHITO: Munthu wake utiyo? EDIPA: Uyu wayima apayu. Unayamba wamuwonapo? WANTCHITO: Aa, sindikumukumbukira. NTHENGA: Mbuyanga, zimene akunenazi si zodabwitsa chifukwa iye- yu watheratu ndi ukalamba. Ukalambatu umapha chikumbumtima n’kuchititsa munthu kufika poyiwala dzina lake. N’kutheka nayenso anadya mtedza wankhwangwala. Dikirani ndimukumbutse ziwiri zitatu. Sindikukayikira kuti akukumbukira zonse zomwe zinachitika pa nthawi yomwe tinakhala limodzi kumapiri komanso madera ena ozungulira. Iyeyu anali ndi magulu awiri a nkhosa, koma ineyo ndinali ndi gulu li- modzi. Ndinakhala naye limodzi kwa miyezi isanu ndi umodzi, kucho- kera m’nyengo yachisanu mpaka m’nyengo yachilimwe. Nyengo yadzi- nja itafika, ndinatsogolera nkhosa zanga kumakola ndipo nayenso ana- kusira nkhosa zake kumakola a Mfumu Layasi. Kodi zimene ndikune- nazi ndi zowona m’bale wanga? WANTCHITO: Mukunena zowona ndithu. Kungoti ndinayiwala, monga mukudziwira kuti ndi kale limene lija. NTHENGA: Usadandawule mnzanga, zimachitika. Ndiyetu ndiwuze ngati ukukumbukira zimene zinachitika pamene unkandipatsa mwana wakhanda uja kuti ndizikamulera ngati wanga. WANTCHITO: N’chifukwa chiyani mukufuna kuti ndikuwuzeni nkhani 38