Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 42

Sewero la Mfumu Edipa kuti asakulole kudziwa chowonadi chokhudza kumene unachokera. EDIPA: [Ak uyank hula nd i gulu la anthu.] M’modzi wa inu apite kuka- tenga m’busa wankhosayo mwamsanga. Musiyeni Yokasi, akuwoneka kuti amamva kukoma kwambiri kukhala mfumukazi. YOKASI: Inu ndiye mavuto sadzakuchokani ayi. Ine sindikuletsaninso, chitani zimene mukufuna. Komanso sindidzakuyankhulitsaninso. [YOKASI akuchoka chothamanga n'kukalowa m'nyumba yachifumu.] WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: N’chifukwa chiyani mfumukazi yachoka ndi nkhope yakugwa? Ndikuganiza kuti tikumana ndi mphepo yamavuto chifukwa cha kukhumudwa kwakeku. EDIPA: Mphepo imeneyotu iwombe! Musiyeni achite zimene akufuna. Kaya ndinabadwira banja losawuka chotani, ndikumba mpaka nditape- za mitsitsi ya kumene ndinachokera. Mwina Yokasi wakwiya chifukwa akuchita manyazi ndi banja limene ndinabadwira. Zikuwoneka kuti amafuna amuna ochokera m’mabanja olozeka. Koma ineyo sindinga- nyozeke chifukwa choti abale anga ndi osawuka. Ndipo ndi wodala mayi amene anabereka ine. Ndi odalanso azichimwene komanso aziche- mwali anga. Sindikukayikira kuti angasangalale kwambiri atandiwona nditakula komanso ndili ndi mphamvu zambiri chonchi. Sindinganyoze kumene ndinachokera ngakhale kutakhala kochititsa manyazi bwanji! [Kenako akuponya maso ake chapatali.] Anthuni, ngakhale sindinayambe nda- wonapo munthu amene tikumudikirayu, ndikuganiza kuti ndi uyo aku- bwera apoyo. Ngati munayamba mwamuwonapo, sindikukayikira kuti mungamuzindikire kwambiri kuposa ine. WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Inde, munthu ameneyu ndiku- mudziwa. Anali wantchito wodalirika wa Mfumu Layasi. [Akufika WANTCHITOYO, ndi wachikulire.] EDIPA: Iwe nthenga wochokera ku Korinto, ndiyambe ndi kukufunsa iwe: Kodi munthu umanena uja ndi ameneyu? NTHENGA: Inde ndi yemweyu ndithu. EDIPA: Iwe munthu wachikulire. Tandiyang’ana ndipo unene zowona zokhazokha. Kodi n’zowona kuti m’mbuyomo unali wantchito wa 37