Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 41

Sewero la Mfumu Edipa NTHENGA: Musafunse ine mlendo, ndikuganiza kuti inuyo ndi amene mungadziwe kumene ali. EDIPA: [Ak utem benuk ira k u gulu la anthu.] Kodi pali aliyense pano amene akudziwa munthu amene akunenedwayu? Munayamba mwa- muwonapo kwinakwake? Ngati pali amene akudziwa chonde anene. Zimenezi zingandithandize kudziwa tanthawuzo la mavuto akuchiti- kawa. WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Munthutu akumutchulayo ndi uja mwatuma kale munthu kuti akamuyitane. Bwanji osawafunsa akazi anuwo? Iwowatu ndi amene akuyidziwa bwino kwambiri nkhaniyi. EDIPA: Yokasi, kodi umadziwa zotani zokhudza munthu wapita kuka- yitanidwa uja? Ndi yemwedi nthengayu akunena? YOKASI: N’chifukwa chiyani mukungokhalira kundifunsa mafunso? Ingoyiwalani nkhaniyi. Mukapitiriza mungodzikalasulirapo mavuto! EDIPA: Zimene wanenazi zikusonyeza kuti munthuyu akunena zowona. Ndiyitsata nkhaniyi mpaka kumutu. Ndikufunika kudziwa zowona zenizeni zokhudza kubadwa kwanga. YOKASI: Chonde musachite zimenezo! Ngati moyo wanu mumawuko- nda, siyiranitu kuyitosa nkhaniyi. Ingololani kuti ineyo ndivutike, zime- nezo zikhala zokwanira. Koma mukapitiriza kuwumitsa khosi muputa mavuto osaneneka. EDIPA: Osadandawula. Ngakhale zitapezeka kuti makolo anga ndi aka- polo, iweyo sizikukhudza. YOKASI: Ndimvereni chonde, ndagwira mwendo wanu! Musachite zi- menezi. EDIPA: Komatu ndikuwuze Yokasi, ngakhale utatani ine sindisintha ma- ganizo. Ndikufuna kudziwa makolo anga enieni. YOKASI: Komatu ndikunena izi pofuna kukutetezani. EDIPA: Zimene ukundiwuzazi zikungochititsanso kuti mutu wanga uwire kwambiri. YOKASI: Oo, munthu wotembereredwa iwe! Ndikupempha mulungu 36