Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 40

Sewero la Mfumu Edipa EDIPA: Kuteroko munali m’busa waganyu? NTHENGA: Inde, komatu ngakhale zili choncho ndi ineyo amene ndina- kupulumutsani. EDIPA: Ndiye mutanditola, ndinkawoneka bwanji? Ndinali bwinobwi- no? NTHENGA: Yang’anani akakolo anuwo muwone mmene munkawonekera. EDIPA: Aa, n’chifukwa chiyani mwatchula tsoka langa lakalekale? NTHENGA: Ndinakupezani akakolo anuwo atabowoledwa ndi chitsulo komanso atakumangani miyendo. Ndi ineyo amene ndinakumasulani. EDIPA: Zipsera zimenezi zimandiwawa kwabasi. Ndakhala ndi zipsera zimenezi kungochokera ndili mwana. NTHENGA: N'chifukwa chaketu anakupatsani dzina muli naloli. 5 5. Dzina lakuti Edipa limatanthawuza "wotuma pamazi." EDIPA: Komano tandiwuzeni, n’chifukwa chiyani makolo anga anandi- chita zimenezi? NTHENGA: Sindikudziwa. Munthu amene anakuperekani kwa ineyo ndi amene anganene zambiri. EDIPA: Mukutanthawuza kuti pali munthu winanso amene anakupatsa- ni mwanayo? Moti simunamutole patchire? NTHENGA: Inde, sindinamutole patchire. M’busa wina ndi amene anandipatsa mwanayo. EDIPA: Mungamukumbukire mutamuwona? Ankaweta nkhosa za nda- ni? NTHENGA: Anthu amati ankaweta nkhosa za Mfumu Layasi. EDIPA: Mukutanthawuza mfumu yomwe inkalamulira kuno zaka za- mbiri zapitazo? NTHENGA: Inde. Zikuwoneka kuti anali wantchito wa Mfumu Layasi. EDIPA: Adakali ndi moyo m’busayo? Ngati ndi choncho, mumadziwa kumene amakhala? 35