Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 39

Sewero la Mfumu Edipa kuti ulosi wa Apolo ukwaniritsidwe pa ine. NTHENGA: Kuteroko kuthawathawa konseku munkawopa kukwatira mayi anu komanso kupha bambo anu? EDIPA: Ndi momwemo ndithu, moti sindigona tulo ndi nkhani imeneyi. NTHENGA: Koma mukudziwa kuti mantha amenewa mumangowona kukhala nawo? EDIPA: Mukutanthawuza chiyani? Mesa makolo anga ndi . . . NTHENGA: Chifukwa chake ndi choti palibe ubale uliwonse pakati pa inuyo ndi a Polebasi. EDIPA: Koma ndiye mwandipindatu pamenepo! A Polebasi si bambo anga? NTHENGA: Iwowo n’chimodzimodzi ineyo. Monga mmene zilili kuti ineyo si bambo anu, ndi mmene zilili ndi a Polebasi. EDIPA: Bwanji mukudziyerekezera ndi bambo anga? NTHENGA: Nkhani ndi yakuti, a Polebasi alowa m’mandawa si bambo anu ngati mmene zilili kuti ineyo si bambo anu. EDIPA: Nanga n’chifukwa chiyani ankanena kuti ndine mwana wawo? NTHENGA: Ngati mukufuna kudziwa ndikhoza kukuwuzani. Ineyo ndi amene ndinakuperekani ngati mphatso kwa iwowaja kuti azikulelani. EDIPA: Komatu ankandikonda kwambiri. Zikanatheka bwanji kuti azi- ndikonda choncho ngati sindinali mwana wawo weniweni? NTHENGA: Chifukwa chake ndi choti ndisanakuperekeni kwa iwowo, akazi awo aja anali owuma. Anakhala zaka zambirimbiri wopanda mwana. N’chifukwa chake ankangokuwonani ngati mwana wawo weniweni. EDIPA: Mwafotokoza kuti munandipereka kwa a Polebasi ngati mpha- tso, koma nanga inuyo munanditenga kuti? Munangonditola penapake? NTHENGA: Ndinakutengani kumapiri. EDIPA: Munkakataniko kumapiriko? NTHENGA: Ndinkaweta nkhosa za mbuye wanga. 34