Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 38

Sewero la Mfumu Edipa EDIPA: Dzina lawo ndi a Merope, akazi a bambo anga a Polebasi. NTHENGA: N’chifukwa chiyani mumachita nawo mantha mayi anuwo? EDIPA: Bambo, ineyo ndinawuzidwa ulosi winawake wochititsa mantha kwambiri. NTHENGA: Ndi nkhani yachinsinsi kapena mukhoza kundibenthulira- ko? EDIPA: Ayi, ndikhoza kukunyotsoleraniko pang’ono. Apolo anandiwu- za kuti ndidzapha bambo anga n’kukwatira mayi anga. Chimenechi n’chifukwa chake zaka zambiri zapitazo ndinathawa kwathu ku Korinto. Nditabwera kuno, zinthu zinayamba kundiyendera bwino monga mme- ne mukuwoneramu. NTHENGA: Ndiye mukutanthawuza kuti munathawa ku Korinto chifukwa chowopa kukwatira mayi anu? EDIPA: Inde, komanso ndinkawopa kuti ndikhoza kudzapha bambo anga. NTHENGA: Mbuyanga, popeza ndabwera kudzakuwuzani uthenga wosangalatsa, bwanji ndikumasuleninso kunsinga za mantha amenewo? EDIPA: Inde, ungachite bwino kwambiri. Ndiwuze chonde ulandira chiwongoladzanja. NTHENGA: Musandandawule ndi zachiwongoladzanjazo, ineyo nda- bwera kudzakutengani kuti mubwerere kwanu ku Korinto. Anthu aku- kuyembekezerani kuti mukakhale mfumu yawo. EDIPA: Ayi. Sindikufuna kubwerera kwathu mayi anga akadali moyo. NTHENGA: Mwana wanga, zikuwonekatu kuti sukudziwa chimene ukuchita . . . EDIPA: [Ak um ud ula maw u nthengayo .] Mukutanthawuza chiyani? Ta- ndiwuzeni bwinobwino musamangondisiya m’malere! NTHENGA: . . . ngati mukukhala moyo wothawathawa n’kumawopa kubwerera kwanu pachifukwa chimenecho, ndikufuna ndikuwuzeni kuti mukungotaya nthawi yanu komanso mukungodzivuta. EDIPA: Ayi sindikudzivuta. Ndikuchita zimenezi chifukwa sindifuna 33