Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 37

Sewero la Mfumu Edipa Nanga ine ndagwira lupanga n’kuwapha ngati? Kapenatu mwina afa chifukwa choti anandipukwa? Ayi ndithu. Sindidzakhulupiriranso ma- wulosi ochokera kwa owombeza mawula kapena kwa aneneri omwe akasowa zochita amayamba kuwuza anthu mabodza. Imfa ya bambo anga yanditsimikizira kuti anthu amenewa ndi atambwali otheratu. YOKASI: Inetu ndinakuwuzani. EDIPA: Indedi unanena, koma kungoti mantha ndi amene anandiphi- mba m’maso. YOKASI: Ndiyetu lekani kuda nkhawa ndi mawulosi osachitikawa. EDIPA: Koma chimene ndikuwopa tsopano ndi mayi anga. Mayi anga adakali ndi moyo. Ndikanakonda nawonso akanamwalira mwachangu. YOKASI: Kodi munthu amene akukhala ndi moyo n’kumasankha yekha zochita, angamachitenso bwanji mantha ndi mawulosi osachitika. Akho- zatu kumangokonza mapulani ake n’kumayesetsa kuti zimene akufuna- zo zitheke. Angaderenso nkhawa ndi chiyani? Si nanga tsogolo lake lili m’manja mwake? Ingogwiritsani ntchito moyo wanuwu mwaphindu, chitani zonse zomwe mungathe kuti zinthu zikuyendereni. Osada nkha- wa ndi zan’kutuzi. Munthu amene anakuwuzani kuti mudzakwatira mayi anuyo adzakwatira ambuyake! N’zowona kuti m’maloto anthu ambirimbiri anakwatirapo mayi awo, koma anthuwo anangoziponyera kunkhongo n’kumapitiriza kuchita zinthu zotukula miyoyo yawo ndipo mpaka pano zinthu zikuwayendera bwino. EDIPA: Zonse zimene ukunenazo zikanakhala zomveka zikanakhala kuti mayi anga anamwalira. Koma popeza akadapuma, mantha sanga- ndichokeretu chifukwa chilichonse chikhoza kuchitika. YOKASI: Komabe, imfa ya bambo anuyi yatikhazika mitima pansi. Yati- thonthoza kwabasi. EDIPA: Indedi, nkhani imeneyi ndi yosangalatsa kwambiri. Atsala ndi mayi anga okhawo basi. Akangomwaliranso amenewa mpamene ndita- yambe kugona tulo tabwino chifukwa sipakhalanso munthu wondiyika pachiwopsezo. NTHENGA: Kodi dzina la mayi anu mukunenawo ndi ndani? 32