Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 35
Sewero la Mfumu Edipa
kuti mutichotsere mavuto atigwerawa. Pakuti tsopano tili ndi mantha
aakulu. Mantha athu ndi aakulu mofanana ndi mmene zimakhalira
anthu akawona amalinyero oyendetsa chombo chimene akwera akulira
pothedwa nzeru ndi namondwe wowopsa.
[YOKASI akuyika nsembe zake paguwa. NTHENGA akulowa. Nthengayu ndi
munthu wachikulire.]
NTHENGA: Wawatu wawa, kodi mungandilozere kunyumba kwa
amfumu? Ndabwera ndi uthenga woti ndiwapatsire.
TSOGOLERI WA GULU LA ANTHU: Nyumba yawo ndi imeneyi ndipo
mwachita mwayi kuti mwawapeza ali pakhomo. Akupereka nsembe
apowo ndiye akazi awo.
NTHENGA: Mulungu akudalitseni mfumukazi yanga ndipo banja lanu
likhale pamtendere mpaka kalekale.
YOKASI: Nanunso mulungu akudalitseni. Mawu anu akusonyeza kuti
ndinu munthu wabwino kwambiri. Ndiye tikuthandizeni bwanji? N’chi-
yani chakubweretsani kuno?
NTHENGA: Mfumukazi yanga, ndabwera ndi uthenga wabwino wopita
kwa mwamuna wanu.
YOKASI: Mwachokera kuti?
NTHENGA: Ndachokera ku Korinto. Ndiye mosachulukitsa gaga, ndi-
kuwuzeni uthenga umene ndadza nawo. Sindikukayikira kuti musanga-
lala nawo kwambiri, ngakhalenso kuti mwina mukhoza kukhumudwa
nawo.
YOKASI: Zingatheke bwanji kuti uthenga umodzi ukhale wosangalatsa
komanso wokhumudwitsa?
NTHENGA: Anthu a ku Korinto akufuna kuti a Edipa akakhale mfumu
yawo kumeneko, moti andituma kuti ndidzawatenge.
YOKASI: Mukutanthawuza chiyani? Mukufuna kundiwuza kuti Mfumu
Polebasi yamwalira?
NTHENGA: Inde, yamwalira ndipo yayikidwa kale m’manda.
YOKASI: Mwati bwanji? Bambo a mwamuna wanga amwalira?
30