Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 34

Sewero la Mfumu Edipa EDIPA: Ngati zimene anganene zikufanana ndendende ndi zimene wafotokozazi, ndiye kuti mavuto alipo. YOKASI: N’chiyani chomwe chili chapadera pa zimene ndakuwuzanizi? EDIPA: Si paja wandiwuza kuti munthuyo ananena kuti Layasi anaphe- dwa ndi gulu la achifwamba. Ngati atanena zofanana ndi zimenezi ndi- ye kuti si ine amene ndinapha Layasi, chifukwa palibe munthu amene angalephere kusiyanitsa munthu m’modzi ndi gulu la anthu. Koma aka- ngonena kuti anaphedwa ndi munthu m’modzi, ndiye kuti mlandu umenewo ugwera pamutu panga. YOKASI: Komatu zimenezo ndi zimene anandiwuza. Ndipo ndikuga- niza kuti sangasinthe poyerayera. Mzinda wonse unamumva akunena zimenezi. Koma ngakhale atasintha zonena, sizingasinthe chilichonse n’kuchititsa kuti ulosi umene Layasi anawuzidwa ukwaniritsidwe. Chi- fukwatu Apolo ananena kuti Layasi adzaphedwa ndi mwana yemwe adzabereke ndi ine. Nanga mwana watsokayo ali kuti? Si anafa kalekale? Kwa ineyo sindikufunikanso umboni wina wonditsimikizira kuti ulosi- wu unalephereka mochititsa manyazi. EDIPA: Zimene ukunenazo ndi zowona. Komabe ndingakonde kuwona- na ndi wantchitoyo basi. YOKASI: Musadandawule mbuyanga, abwera. Koma panopa tiyeni kaye mukalowe m’nyumba. [EDIPA ndi YOKASI akulowa m'nyumba yachifumu. Kenako YOKASI akutu- luka limodzi ndi akapolo ake awiri n’kupita pamene pali guwa lansembe la Apolo lomwe lili pafupi ndi khomo lolowera m’nyumbayo.] YOKASI: Inu akuluakulu a Thebesi, ndawona kuti ndi bwino ndidzape- mbedze milungu yathu pamaguwa opatulikawa. Ndachita zimenezi chifukwa a Edipa ali ndi nkhawa yayikulu komanso asokonezeka maga- nizo. Iwo akungoganizira zimene zinachitika kalekale m’malo mopeza njira yothetsera mavuto akungowunjikanawa. Zikuwoneka kuti sakuga- nizanso bwinobwino. Akungomvetsera munthu aliyense amene akuwa- fotokozera uthenga wochititsa mantha, moti asiya kumvetsera zonena zanga. [Ak uyam ba k up em p hera.] Apolo, tabwera kudzalira pamaso pa- nu. Tabwera kwa inu ndi nsembe komanso zofukizira ndipo tikupempha 29