Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 54

Sewero la Mfumu Edipa nda makolo. [Akuyankhula ndi gulu la anthu.] Anthu a ku Thebesi, awa akhala ana anu tsopano. Musalole kuti akule movutika. Musayiwale kuti mwana wa mnzako ndi wako yemwe, ukachenjera manja umadya naye. Chonde asamalireni asadzafe mbeta. Nawonso ndi abale anu, musalole kuti adzamve zowawa zangati ndakumana nazo inezi. Ndagwira mwendo wanu, chonde amvereni chisoni. Tawonani misinkhu yawoyi, adakali anthete ndipo akumana kale ndi mavuto oposa misinkhu yawo. Ndilo- njezeni kuti muziwathandiza. Ndiponso inu ana anga, pali zinthu zambiri zimene ndikanakonda nditakuwuzani, koma sinditero pakuti ndinu ana. Koma ndikukupemphani kuti muyesetse kuti musadzakhale ndi moyo wovuta ngati wangawu. KIREYO: Basi mwalira mokwanira, pitani mukalowe m’nyumba. EDIPA: Ndikumvera ngakhale kuti si zimene ndimafuna. KIREYO: M’kupita kwa nthawi, zinthu ziyambiranso kuyenda bwino. Osadandawula. EDIPA: Ndipitadi, koma choyamba ndikufuna ulumbire kaye. KIREYO: Mukufuna ndilumbire chiyani? EDIPA: Lumbira kuti undichotsa kuno, sindikufunanso kukhala ku Thebesi kuno. KIREYO: Ndi mulungu yekha amene angakuchitireni zomwe mukufu- nazo. EDIPA: Ukutanthawuza kuti wavomera? KIREYO: Musandiyike mawu mkamwa. Ine sindikufuna kumayankha ndisanaganize. Ndimawopa kudzilowetsa m’mavuto. EDIPA: Ndiyetu nditulutse mumzinda muno kuti usalowe m’mavuto- wo. KIREYO: Chabwino, koma musatenge anawa. EDIPA: Ayi, sindilola zimenezo. Ukuganiza kuti ukandilanda anawa ndiye nditsala n’chiyani? KIREYO: Musayiwaletu kuti mulibenso mphamvu zomangolamula 49