Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 55

Sewero la Mfumu Edipa chimene mukufuna. Sinunso mfumu ayi, ndinu munthu wamba. [KIREYO, EDIPA, ANTIGONE, ISIMENE ndi ANTCHITO aja akulowa m'nyumba yachifumu ndipo sewero likuthera pomwepo.] 7 7. Sewereoli limatha zisakudziwika bwinobwino kuti Edipa anachokadi ku Thebesi kapena ayi. Malinga ndi nthano zina zakale kwambiri zomwe Sophocles anagwiritsa ntchito polemba seweroli, Edipa anakhalabe ku Thebesi kwa kanthawi mzika komanso Kireyo asanamuthamangitse mumzindawo. Komanso zimene Kireyo ananena chakumapetoku, zikusonyeza kuti anakonza zoti adikire mpaka atamva kuchokera kwa Apolo zenizeni zoti achite ndi Edipa. Komabe zimawoneka kuti m'buku lina lotchedwa Illiad, Homber analemba kuti Edipa anafera ku Thebesi ndipo pamaliro ake anthu a ku Thebesi anachita miyambo komanso masewera osiyanasiyana pomulembekeza. 50