Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 53

Sewero la Mfumu Edipa uwasamalire bwino mpaka atakula. Koma choyamba alole kuti abwere adzagwire manja angawa ndisananyamuke kuti ndilire nawo limodzi. Kireyo m’bale wanga, iwe munthu wamtima wabwino, ngati nditawa- gwira ndi manja angawa, kulikonse kumene ndingapite ndiziwakumbu- kira. [ANTCHITO ena ak ufik a nd i ANTIGONE k o m anso ISIMENE k u- chokera m'nyumba yachifumu.] Ndikumva kuti kukubwera anthu, kodi ndi ana anga okondedwa amene akulirawo . . . ? Kodi Kireyo wandichitiradi chifundo ponditumizira ana anga, ana omwe ndimawakonda kwambiri? Kodi ndi zimenedi zikuchitika? 6. Ana aamuna awiri a Edipa ndi Utiko komanso Polenike ndipo ayenera kuti pa nthawiyi anali ndi zaka khumi mphambu zisanu kapena zaka khumbi mphambu zisanu ndi chimodzi ndipo sanali aakulu moti n'kukhala pampando wa bambo awo monga mfumu. KIREYO: Inde. Ndawabweretsa kwa iwe kuti uwakumbatire. Ndiku- dziwa kuti ana amenewa umawakonda kwambiri ndipo mwina mtima wako ungapepukeko. EDIPA: Ndimakukondani ana anga moti ndikukufunirani zabwino zo- nse. Ndikupempha kuti mulungu akuyang’anireni komanso akuchitireni zabwino osati zangati zimene zachitikira inezi. Ana anga, kodi muli ku- ti? Bwerani kuno, bwerani ndikukumbatireni. Inuyo ndinu azichemwali anga tsopano. Gwirani manja omwe achotsa maso angawa n’kuwachi- titsa kuti aziwoneka mdima wandiweyani. Tawonani pomwe panali maso anga pangotsala zigompholera zokha. Ineyo ndinali bambo yemwe ngakhale ndinali ndi maso sindinkapenya, moti mosadziwa ndinabereka inu ndi mayi omwe anandiwonetsa dzikoli. Pepani kwambiri ana anga. Ngakhale kuti pano sindikuthanso kuwona, sindingakuyiwaleni nga- khale pang’ono. Ana anga muvutika chifukwa cha ine moti mwina anthu ena azikusalani, sazikuyitanani m’mapwando awo. Mukafika msinkhu wokwatiwa, ndikuda nkhawa kuti mwina sipadzapezeka mu- nthu woti akukwatireni chifukwa cha zinthu zochititsa manyazi zomwe bambo wanune ndinachita. Pepani kuti munachita tsoka kukhala ndi bambo wotembereredwa ngati ine. Bambo anu anapha bambo awo, ndi- po kenako anakwatira mayi awo ndipo anabereka inuyo. Anthu aziku- nyozani kwambiri chifukwa cha zimenezi. Ndiye ndi ndani angalimbe mtima kuti akukwatireni? Palibe ana anga. Inuyo mudzakula mpaka kuchita chisira ndipo mudzafa muli mbeta. Ana atsoka inu, mukula opa- 48