Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 52

Sewero la Mfumu Edipa kundichitira chifundo, ndichotse ku Thebesi kuno. Ndithamangitsire kumalo omwe sikukhala munthu aliyense komanso kumene sikungafike munthu. KIREYO: Zimenezo ndichita ndithu, koma choyamba ndikufuna ndimve kaye maganizo a mulungu wathu. EDIPA: Komatu paja Apolo ananena kale zomwe tikuyenera kuchitira munthu amene wabweretsa tsokali. Anati munthu ameneyo akuyenera kuwonongedwa. Tsopanotu zadziwika kuti munthu ameneyo ndi ineyo, ndiye n’chifukwa chiyani ukuzengereza? KIREYO: Sindikuzengereza, ndichita momwemo ndithu. Komabe ndi zimene zachitikazi, tingachite bwino kudziwa zenizedi zimene akufuna kuti tichite. EDIPA: Kodi ukufuna uzikamupempha kuti ndikhalebe ndi moyo mme- ne ndililimu? KIREYO: Zimenezo ndiye zoyenera kuchita. Ndipo nanunso mukufuni- ka kuyamba kukhulupirira kwambiri milungu. EDIPA: Inde, ndikuyeneradi kutero. Ndiye ndili ndi ntchito yoti uchite usanakapemphe zimenezi. Mayi uyo ali m’nyumbayo, chonde umuko- nzere mwambo wamaliro. Iweyo ndi amene uli ndi udindo wochita mi- yambo yonse yamaliro popeza ndi mchemwali wako. Koma usayerekeze kuchititsa kuti mzinda wa bambo anga ukhale wodetsedwa chifukwa choti ine ndikupitirizabe kukhala kuno. Ndilole kuti ndizipita kuti ndi kakhale kumapiri a Katero, komwe ndinakatayidwa. Pamene bambo anga ndi mayi anga anali moyo, anasankha kuti manda anga akakhale kumeneko. Choncho ndikufuna kukafera kumeneko potsatira zomwe makolo anga ankafuna. Koma chimene ndikudziwa n’choti sindifa ndi matenda kapena mavuto ena aliwonse. Ndikudziwa kuti sindingadzafe popanda chinachake chowopsa kundichitikira. Koma kaya ndidzafa bwanji, ndisiyeni ndichoke kuno. Ponena za ana anga aamuna awiri, sindikusenzetsa udindo woti uziwasamalira, chifukwa akula tsopano. Ndikudziwa kuti akhoza kudzisamalira pawokha tsopano. 6 Koma pone- na za ana anga aakazi awiri omwe sanazolowere kukhala popanda ine, omwe ankadya chakudya chomwe ndinkadya, ndikukupempha kuti 47