Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 51

Sewero la Mfumu Edipa itatu, iwe amene unayamwa magazi a bambo anga omwe ndinawakhetsa ndi manja anga, kodi ukundikumbukirabe? Kodi ukukumbukira zimene ndinachita pamaso pako komanso zomwe ndinachita nditabwera kuno ku Thebesi? Aa, ndi kotembereredwa kubadwa kwanga! Tawonani mi- mba imene ndinachokera inaberekanso ana ena. Ana a ine munthu ye- mwe ndinachokera m’mimba yomweyo. Tawonani ndinapanga banja lobweretsa chitonzo la anthu apachibale. Tandiwuzani anthuni, palinso chonyansa china chomwe chingapose pamenepa? Chonde ndichotseni kuno mwansanga, kandibiseni kudziko lina kunja kwa mzinda wa Thebesi. Mukhozanso kungondipha, kapena kundimangirira chimwala champhero m’khosi n’kukandiponya m’nyanja kuti ndisadzawonekenso mpaka kalekale. Bwerani, mugwire thupi la munthu wotembereredwa. Musachite nane mantha popeza nthenda yomwe ndikudwala ndi yoti singagwirenso munthu wina. WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Kireyo akubwera. Ndikuwona kuti wabwera pa nthawi yake kuti achite zimene a Edipa akutipemphazi. Popeza akuchoka, Kireyo ndi amene watsala amene angateteze mzinda wathuwu. EDIPA: Kalanga ine, ndikwanitsa bwanji kuyankhula naye? Ndimuwuza chiyani kuti andikhululukire? Si kale pamene ndinamuchititsa kumva zowawa. [Akufika KIREYO.] KIREYO: A Edipa, ndabwera kuti ndidzakuyimbeni mlandu pa zimene munandichitira. Koma choyamba, ngati moyo wayamba kukunyansani, chonde lemekezani mulungu wathu dzuwa, yemwe amachititsa kuti zinthu zimere ndipo musawonetse anthuwa chonyansa chotere. Chifu- kwatu ngakhale dziko kapena kuwala kapena mvula yopatulika singa- kondwere ndi zimene mwachitazi. [KIREYO ak uyam ba k uyank hula nd i antchito.] Tawatengani awa mulowe nawo m’nyumbamu mofulumira. Chinthu chabwino kwambiri chimene tingawachitire ndi kuwalola kuti awonane ndi ana awo kuti awawuze mawu omaliza. EDIPA: Kireyo ndiwe munthu wabwino kwambiri. Sindimaganiza kuti ungandichitire zinthu mwachifundo chonchi. Koma ngatidi ukufuna 46