Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 31

Sewero la Mfumu Edipa EDIPA: Panopa sindilinso moti n’kumayankha mafunso a munthu. Ta- ndiwuze, kodi Layasi anali wowoneka bwanji? Nanga anali ndi zaka zingati pamene ankaphedwa? YOKASI: Anali wamtali komanso wachikulire, moti imvi zinali zitaya- mba kumutu kwake. Mawonekedwe ake sanali osiyana kwenikweni ndi mmene mumawonekera inumu. EDIPA: Koma ine ndili ndi tsoka lalikulu! Zikhoza kuthekatu kuti ndina- kwaniritsa ulosi wochititsa mantha uja mosazindikira. YOKASI: Mukutanthawuza chiyani mbuyanga? Zimene mwayamba ku- chitazitu zayamba kundichititsa mantha? EDIPA: Nanenso ndili ndi mantha aakulu kwambiri. Komabe, ndikuga- niza kuti ndikhoza kudziwa zowona zake ngati utandiyankha funso linanso limodzi. YOKASI: Nanenso ndasokonezeka maganizo, komabe funsani. EDIPA: Kodi pawulendowo Layasi anapita ndi anthu ochepa kapena anapita ndi gulu la asilikali monga zimakhalira ndi mfumu? YOKASI: Anapita ndi amuna asanu, kuphatikizapo nthenga m’modzi. EDIPA: Kalanga ine! Zonse zimene ukunenazo ndi zowona. Ndi ndani anakuwuza zimenezi? YOKASI: Wantchito wa Layasi, yemwe anapulumuka pachiwembucho. EDIPA: Watchitoyo amakhala kuti? Amagwirabe ntchito m’nyumba yathuyi? YOKASI: Ayi. Atangobwera n’kumva zoti inuyo mwalongedwa ufumu m’malo mwa Layasi, anandichonderera kuti ndimulole achoke kuno. Ankati ndimutumize kubusa azikaweta nkhosa zathu. Iye sankafunanso kukhala pakati pa anthu a ku Thebesi kuno. Nditawona chisoni chimene anali nacho, ndinangomulola kuti achite zimene ankafunazo. N’zowona kuti anali kapolo, koma zomwe anachita zinandikhudza kwambiri, moti ndinamuchitira chifundo. Ndimawona kuti ankafunika kumuchitiranso zoposa pamenepo. EDIPA: Ndikufuna abwere kuno msanga, muyitanitse abwere pompa- 26