Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 32

Sewero la Mfumu Edipa nopompano. YOKASI: Mkazi wanga, ndikuchita mantha kuti ndayankhula kale za- mbiri. N’chifukwa chake ndikufuna kuti munthu ameneyo abwere mwa- msanga. YOKASI: Chabwino abwera posachedwapa. Koma tsopano mbuyanga, chonde ndiwuzeni chimene chikukudetsani nkhawa chonchi. EDIPA: Nkhawa yomwe ndili nayo yandikulira moti sindikubisiranso chilichonse. Kwa ineyo palibenso wina yemwe ndingamuwuze zaku- khosi kwanga kuposa iweyo. Bambo anga ndi a Polebasi a ku Korinto, pomwe mayi anga ndi a Marope a ku Doriya. Chifukwa cha mphamvu zimene ndinali nazo kwathu, anthu ankandilemekeza kwambiri kufikira pamene mnzanga wina woledzera anayamba kundinena kuti ndine mwana wopanda bambo komanso mayi. Ankati a Polebasi si bambo anga enieni. Ndisanameyi, nkhani imeneyi inandisokoneza maganizo kwambiri. N’zowona kuti sindinamuyankhe, koma ndinachita zimenezo modziletsa kwambiri. Tsiku lotsatira ndinapita kwa makolo anga n’ku- kawafotokozera nkhaniyo. Atamva zimene zinachitikazo, nawonso ana- kwiya kwambiri. Iwo ananditsimikizira kuti ndine mwana wawo. Koma- be, kamtima kena kankandiwuzabe kuti ndipitirize kufufuza nkhaniyo. Chomwe chinkandiwawa n’choti mbiri ya nkhaniyo inali itawanda mu- mzinda wonse. Choncho ndinaganiza zopita ku Defi mwachinsinsi kuti ndikafufuze zowona zake. Koma sindinawuze mayi komanso bambo anga. Nditafika ku Defi, Apolo sananene chilichonse chomveka. Anka- ngondiwuza zinthu zodabwitsa zokhazokha. Ankati ndidzachita zinthu zochititsa manyazi kwambiri komanso ndidzakumana ndi mavuto osa- neneka. Ananenanso kuti ndidzapha bambo anga n’kukwatira mayi anga, kenako n’kubereka nawo ana. Nditamva zimenezi, ndinatsimikiza mtima kuti sindidzabwereranso ku Korinto. Kungochokera tsiku lime- nelo, ndinasiyiratu kukutenga ngati kwathu. Posafuna kuti ulosiwu ukwaniritsidwe pa ine, ndinayamba kukhala moyo woyendayenda. Pa- mene ndinkathawa themberero limenelo, ndinadutsa pamalo ena omwe panakumana misewu itatu. Pamenepo ndinakumana ndi anthu akuye- nda pambali pagaleta lokokedwa ndi mahatchi. M’galetalo munali mu- nthu wachikulire, yemwe anali ndi mawonekedwe ofanana ndi amene 27