Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 29

Sewero la Mfumu Edipa YOKASI: Inde, ndiwaperekeza ndikadziwa chimene chadzetsa mpu- ngwepungwewu. MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Amakambirana zinazake, ndiye zinangopezeka kuti ayamba kukangana. Ndikuwona kuti zimenezi za- chitika chifukwa sakumvetsetsana. YOKASI: Onse awiri? MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Inde. YOKASI: Chatsitsa dzaye n’chiyani? MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Ndi mavuto akuchitikawa, ndi- kuwona kuti ndi bwino nkhaniyi tingoyisiya. EDIPA: Wawonatu kuwopsa kwa nkhaniyi, si choncho? Ukuzindikira zimenezi utandifowoketsa kale kuti ndisapereke chilango kwa munthu amene akufuna kundipha. MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Mbuyanga mfumu, ndanena ka- le mobwerezabwereza kuti kungakhale kupanda nzeru kuyamba kuli- mbana nanu kapena kukugalukirani. Inuyo munatipulumutsa mzinda- wu uli pamavuto adzawoneni ndipo zinthu zinayamba kuyenda bwino. Timakudalirani kwambiri ndipo timawonani monga mpulumutsi wathu. YOKASI: Chonde mbuyanga, ndiwuzeni chimene chachititsa kuti mupse mtima chonchi. EDIPA: Iweyo mkazi wanga ndimakudalira kuposa anthu enawa. Ndiye ndikuwuza chilungamo. Vuto ndi Kireyo. Kireyo akundikonzera chiwe- mbu. YOKASI: Ndiye n’chiyani chinachititsa kuti mufike pokangana choncho? Tandiwuzeni zonse. EDIPA: Kireyo amanena kuti ineyo ndi amene ndinapha Mfumu Layasi. YOKASI: Anakuwuzani kuti wachita kumva nkhaniyi kwa winawake, kapena anakuwonani mukuchita zimenezi. EDIPA: Ayi, anagwirizana ndi mneneri wonyenga uja kuti adzandiwuze zimenezi. Ndiye wabwera pano n’kuyamba kuwusasa mlanduwu ngati kuti m’manja mwake ndi moyera. 24