Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 27
Sewero la Mfumu Edipa
akubwera moti mungachite bwino kudula kaye mkangano wanuwu.
[YOKASI akufika kuchokera m'nyumba yachifumu.]
YOKASI: Kodi n’chifukwa chiyani anthu akuluakulu ngati inu mukuka-
ngana ngati ana? Simukuwona kuti dziko lanuli lawola ndi mavuto? Zo-
wona simungachite manyazi kumakokanakokananso nokhanokha? A
Edipa, kaloweni m’nyumba. Nawenso Kireyo zipita kwanu. N’chifukwa
chiyani mukutibowola m’makutu ndi nkhani zanu zopanda ncherezi?
KIREYO: Chemwali, mwamuna wanuyu akundiyimba mlandu wowo-
psa kwambiri. Akuti akufuna kundithamangitsa kuno, apo ayi akuti
andinyonga.
EDIPA: Sakunamayi. Mkazi wanga, ndapeza kuti munthu uyu akundi-
konzera chiwembu. Wayamba kugwirizana ndi anthu ena kuti andicho-
tse pampando.
KIREYO: Ndikunenetsa pano kuti ndikhale wotembereredwa ngati zi-
mene akundinenezazi zilidi zowona.
YOKASI: A Edipa, pamaso pa milungu yathu ndikukupemphani kuti
mumukhulupirire mlamu wanuyu. Ngati wafika podzitemberera cho-
nchi ndiye kuti sakunama.
MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Zowonadi, chitani momwemo
ndithu mbuyanga. Mawu amene mkazi wanuyu wanena ndi owona.
EDIPA: Ndiye iweyo ukufuna kuti ineyo nditani?
MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Perekani ulemu umene Kireyo
akuyenera kulandira. Iyeyu sanayambe wakugalukiranipo ndi kale lo-
nse, komanso lumbiro wachita lija ndi loti munthu sangalinene ndi milo-
mo yabodza.
EDIPA: Koma ukudziwa chimene ukunena iwe?
MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Inde, ndikudziwa mbuyanga.
EDIPA: Ndiye ndiwuze mosapita m’mbali chimene ukufuna ndichite.
MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Simukuyenera kuyimba mlandu
mnzanu wapamtima chifukwa cha mphekesera zopanda umboni. Pope-
za mwamumva akulumbira, muyenera mukudziwa kuti akhoza kuku-
22