Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 26

Sewero la Mfumu Edipa EDIPA: Ngati munthu wina akufuna kundiwukira kapena kundipanga chipongwe, ndiyenera kudziteteza. Mmene anthu oyipa mitima akuchu- lukira masiku ano mpofunika kumakhala osamala. Ukapusa ukhoza ku- ngozindikira thupi lako lalowa m’bokosi. KIREYO: Ndiye mukufuna munditani, mundithamangitse kuno? EDIPA: Ayi. Ndikufuna kuti ufe n’cholinga choti ena atengerepo phu- nziro kuti aziganiza kawiri asanayambe kuchitira anzawo nsanje kapena kaduka. KIREYO: Mwatsimikizadi mtima moti simusintha maganizo? EDIPA: Iweyo sungasinthe maganizo anga ndipo sindingayerekezenso kukhulupirira zonena zako. Kukhulupirira munthu ngati iweyo n’chi- modzimodzi kuyika mutu wanga mkamwa mwa ng’ona. KIREYO: Ndikuthadi kuwona kuti panopa simukuganiza bwino. EDIPA: Ndikuganiza bwinobwino bwanawe, moti usanganize kuti ndi- kucheza ayi. Ndikufuna kuteteza moyo wanga. KIREYO: Komatu mukufunikanso kuteteza ineyo. EDIPA: Nditeteza bwanji munthu wosakhulupirika ngati iwe, munthu yemwe umandisekerera kuseri ukundinolera lupanga loti undibaye nalo? Khalidwe lako ndi lochititsa nseru kwabasi. KIREYO: Koma nanga bwanji ngati mukulakwitsa? EDIPA: Ngakhale zitakhala kuti ndikuphonya, zomwe ndagamulazi sizi- ngasinthe. KIREYO: Komatu zinthu sizikutherani bwino ngati mwayamba kulamu- lira mopanda chilungamo choncho. EDIPA: Ayi, Thebesi yense ali m’manja mwanga. Palibe amene angandi- wopseze kapena kundiwuza zochita. KIREYO: Komatu inenso ndi mzika ya Thebesi ndipo ndine mfulu ngati inuyo. Si ine kapolo wa munthu kuti mundichitire zopanda chilungamo chonchi. [Khomo la nyumba yachifumu likutsegulidwa.] MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Pepani olemekezeka, Yokasi 21