Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 24

Sewero la Mfumu Edipa kuti mundiyende pansi, si bwenzi atanena kuti ineyo ndi amene ndinapha Mfumu Layasi. KIREYO: Koma ngati ananena zimenezo, inuyo ndi amene mukudziwa chilungamo chake. Tsopano yafika nthawi yoti nanenso ndikufunseni mafunso. EDIPA: Funsa, palibe amene wakutseka pakamwa. Koma ngati ukuwe- rengera kuti upeza kuti ineyo ndi amene ndinapha Mfumu Layasi ndiye ukungotaya nthawi yako. KIREYO: Chabwino, ndiyankheni kaye funso langali: Kodi inuyo muna- kwatira mchemwali wanga? EDIPA: Ngakhale kuti ukufunsa chinyezi kubafa, ndikuyankha. Inde, ndinakwatira mchemwali wako. KIREYO: Ndipo nonse awiri mumalamulira ndi mphamvu zofanana mumzindamu, si choncho? EDIPA: Inde, chilichonse chimene mkazi wanga akufuna ndimamupatsa mosawumira. KIREYO: Ndipo ineyo ndimalamulira ndi mphamvu zofanana ndi awi- rinu, si choncho? EDIPA: Chimenecho n'chifukwa chake ndinanena kuti kusakhulupirika wachitaku n'kowopsa kwambiri. Sindikumvetsa kuti wachitadi zimenezi ndikaganizira kuti ndiwe m'bale wanga komanso mnzanga wapamti- ma! KIREYO: Komatu zinthu sizili choncho, moti mutaganiza bwinobwino, muwona kuti mukuphonya kwambiri. Choyamba, taganizirani izi: Kodi mukuganiza kuti munthu angasankhe chiyani pakati pa kukhala wola- mulira n'kumavutika ndi nkhawa, ndi kukhala pansi pa ulamuliro wa munthu winawake n'kumasangalala ndi mtendere wam'maganizo ko- manso ufulu, koma ali ndi mphamvu zofanana ndi zimene akanakhala nazo akanakhala wolamulira? Ndikukuwuzani kuti ineyo sindimafuna kukhala mfumu. Ndimasangalala kumagwira ntchito zina zaboma. Ndi- kuwonanso kuti munthu aliyense amene mutu wake umagwira bwino- bwino angaganizenso mofananamo. Panopa ndimapeza chilichonse 19