Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 23

Sewero la Mfumu Edipa kitsa kuti ndiyitanitse Teresi? KIREYO: Inde, ndinaterodi. Ndipo mukanakhala kuti simunamuyitane ndikanakulimbikitsaninso kuchita zomwezo. EDIPA: Kodi patenga nthawi yayitali bwanji kuchokera pamene Mfumu Layasi . . . [Ak uyim a k aye .] KIREYO: Mfumu Layasi yatani? Kodi nkhaniyi ikumukhudza bwanji Layasi? EDIPA: Usandidule pakamwa. Ndafunsa kuti patenga nthawi yayitali bwanji kuchokera pamene Mfumu Layasi inachoka kuno n'kukaphedwa ndi achifwamba? KIREYO: Zinachitika kale kwambiri. Padutsa zaka zambirimbiri. EDIPA: Kodi pa nthawi imeneyo, Teresi anali mlosi wodalirika ngati mmene alili masiku ano? KIREYO: Inde, sanasinthe ngakhale pang’ono. EDIPA: Ndiye tandiwuze, Teresi anayamba waloserapo zokhudza ine? KIREYO: Ayi, sanayambe wakutchulanipo, kusiyapo ngati ananena zi- menezo ine palibe. EDIPA: Mutamva zoti Mfumu Layasi yaphedwa, kodi munayamba kufu- nafuna anthu amene anapha mfumuyo? KIREYO: Inde, tinayamba kufufuza. Koma sitinagwire munthu aliyense. EDIPA: Ndiye n'chifukwa chiyani mlosi wanuyu sananenepo kanthu? Bwanji sanakuthandizeni kupeza anthu omwe anapha mfumuyo? KIREYO: Sindikudziwa. Ndikakhala kuti sindikudziwa zambiri zokhu- dza nkhani inayake, ndimawona kuti ndi bwino kungotseka pakamwa panga n’kukhala chete. EDIPA: Koma uyenera ukudziwapo kanthu. Usandinamize kuti suku- dziwa chilichonse. Ukuyenera kundiwuza . . . KIREYO: Kukuwuzani chiyani? Ndikanakhala kuti ndikudziwapo ka- nthu ndikanakutsanulirani zonse zimene ndikudziwa. EDIPA: Ukunama iwe. Zikanakhala kuti Teresi sanapangane ndi iweyo 18