Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 22

Sewero la Mfumu Edipa chifukwa nthawi zina zimene zimawoneka panja si zimene zimakhala mumtima. Ubwino wake a Edipa ndi awo akubwerawo, mwina muwa- funse akuwuzeni. [EDIPA akutuluka kuchokera m'nyumba yachifumu.] EDIPA: Iwe, ndi ndani wakulola kufika kuno? Kodi watha mantha kuti tsopano ufike pobwera kunyumba kwanga kuno? Ndiwe munthu amene unapha mwini nyumbayi, ndpo zikuwoneka kuti ukufunanso kulanda ufumu wanga? Tabwera kuno undiyankhe, kodi unapangana ndi mne- neri wabodza uja kuti azidzandiwuza phala lakelo poganiza kuti mu- ngandipite pansi? Kapena umaganiza kuti sindizindikira kuti ndiwe tambwali wotheratu yemwe amakhala ngati nkhosa pamaso, mumtima ali m’mbulu wolusa? Kodi zimene ukuyesa kuchitazi ukuganiza kuti zikakufikitsa kuti? Pa moyo wanga sindinayambe ndawonapo munthu wopanda manyazi ngati iwe. Zowona ukuganiza kuti ungalande mpa- ndo wachifumu mophweka choncho? KIREYO: Bwanji mumve kaye mbali yanga musanathe mawu? EDIPA: Ukufuna udziyikire kumbuyo. Ngati ukuganiza kuti ungandi- pusitse ndiye walemba m’madzi. Sungasunthe mtima wanga ndi paka- mwa pako pathererepo. Chomwe ndikudziwa n’choti ndiwe tambwali wotheratu, munthu amene amandimwetulira akundisungira kampeni kumphasa. KIREYO: Chonde yambani mwandimvetsera kaye. EDIPA: Palibenso chimene ungandiwuze, ndiwe munthu wosakhulupi- rika ngakhale pang’ono. KIREYO: Ngati mukuganiza kuti kuvuta kumasonyeza nzeru ndiye kuti nzeru zanu zatayika. Simukuyenera kumaganiza choncho. EDIPA: Nawenso ngati ukuganiza kuti ukhoza kundikonzera chiwembu n’kuzemba chilango, ndiye ukudzinamiza. Iwenso sukuyenera kumaga- niza choncho. KIREYO: Zowonadi. Zimene mukunenazo ndi zowona. Ndiyetu ndiwu- zeni mlandu umene mukunena kuti ndapalamulawo! EDIPA: Unditsutse ngati ndikunama, kodi iweyo si amene unandilimbi- 17