Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 20

Sewero la Mfumu Edipa TERESI: Inetu sindimafuna kubwera kuno, inuyo ndi amene munatuma munthu kuti adzanditenge. EDIPA: Kungoti sindimadziwa kuti mudzayankhula zopusa chonchi. Ndikanadziwa sindikanayerekeza n’komwe. TERESI: N’zowona kuti ndinabadwa wosawona. Koma musaganize kuti ndinachita kufuna. Ndipo ndikuwuzeni pano kuti makolo anu sankawo- na chilema changachi ndipo ankandilemekeza kwambiri. EDIPA: Mwati chiyani? Makolo anga? Mumawadziwa makolo anga inu? TERESI: Dikira ndikuwululireni chinsinsi chonse bwinobwino ndipo chinsinsi chimenechi n’chimene chitakuwonongeni kotheratu. EDIPA: Chakudzerani n’chiyani a Teresi? Mwakhuta chiyani lero? Bwa- nji mukungoyankhula chipwitikizi chokhachokha? Mukuganiza kuti ndinakuyitanani kuti tizidzachita ndagi? TERESI: Pajatu inu ndi katswiri wodziwa kupereka mayankho a ndagi zovuta kwambiri, moti ndikulakalaka muyankhe ndagi ndaperekayi. EDIPA: Inutu mwatumidwa! Tiyeni nazo, muwona kuti palibe amene angasewere ndi ine. TERESI: Nzeru zanuzo ndi zimene zitakuwonongeni. EDIPA: Ndilibe nazo ntchito! Tiwona amene atawonongeke. TERESI: Basi ndilekeni ndizipita kwathu ine. Mnyamata, ndilondolere njira! EDIPA: Inde, akufunikadi akulondolereni njira. Mukakhalabe pano mu- ngotiphulitsapo ngozi. TERESI: Koma ndisanapite ndikufuna ndikuwuzeni kaye chimene chi- nandichititsa kuti ndibwere ngakhale sindimafuna. Ineyo sindikuchita mantha ndi nkhope yanu yokwiyayo chifukwa palibe chimene munga- ndichite. Ndakuwuzani kale kuti, munthu amene mwakhala mukumu- funafuna nthawi yonseyi ali pompano. Malinga ndi zimene ndikudziwa, munthuyo ndi mlendo amene amakhala kuno. Koma mukafufuza mupe- za kuti si mlendo ayi. Ndi mbadwa ya ku Thebesi konkuno. Munthuyo akangozindikira zimenezi moyo wake uwonongekeratu. Achita khungu, 15