Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 18

Sewero la Mfumu Edipa Bwanji mumangokhala ngati matupi anu anapangidwa ndi nsanje yo- khayokha. Mukufuna mundichotse pampando n’cholinga choti mukha- lepo. Inetu sindinachite kuwumiriza anthu kuti andilonge ufumu. Okha anachita kundikakamiza atawona ntchito zanga zakupsa. Ndakhumu- dwa kwambiri kuzindikira kuti Kireyo, mnzanga komanso m’bale wa- nga weniweni, akundikonzera chiwembu kuti andichotse pampando ndipo wagwirizana ndi wansembe wachinyengoyu, yemwenso ndi wo- sawona kotheratu kuti andiwukire. Wansembe yemwe ndi khungu la- kelo amangowona zinthu zokhazo zomwe zingamupindulitse. Ngati akutsutsa zimene ndikunenazi andipatse umboni womveka bwino. Ndi- po inuyo monga wansembe, kodi munali kuti pamene chilombo choyi- mba chija chinkazunza komanso kupha anthu kuno? Palibetu munthu amene ankadutsa pamaso pake popanda kupereka yankho lolondola la ndagi yake ija ndipo ambiri anadibwa chifukwa chochita masewera amenewa. Koma inuyo simunanene chilichonse kuti muwapulumutse. N’chifukwa chiyani sumunawathandize kupereka yankho lolondola la ndagiyo? N’chifukwa chiyani anthu sanabwere kwa inu monga mneneri wawo kuti muwathandize? Anthuwotu ankadziwa kuti ndinu mneneri wopanda phindu, yemwe amangodendekera mutu wake n’kumanamiza anthu kuti amawona zinthu zomwe ena sangaziwone chonsecho maso ake ndi akhungu. Koma tawonani ineyo munthu yemwe sindinkadziwa chilichonse, ndinabwera kuno n’kugonjetsa chilombocho ndi nzeru za- nga popanda kudalira mbalame zolosera. Anthu atawona ubwino wa- nga, anandilonga ufumu. Ndiye lero mungodzuka uko, manthongo ali bwito-o m’manso, nkhongo zili gwa, n’kumanena kuti ndine amene ndinapha Layasi, zachamba eti! Kuteroko mukuwerengera kuti Kireyo akakhala mfumu adzakupatseni mpando wonona kuti muzidzadya bwino? Chomwe ndikudziwa n’choti nonse munong’oneza bondo ndi zimene mukuchitazi. Zikanakhala kuti si inu wokalamba chonchi, bwe- nzi mutalandira chilango chokhwima kwambiri kuti mutengerepo phu- nziro. WOTSOGOLERA GULU LA ANTHU: Kwa ifeyo, zikuwoneka kuti a Teresi ayankhula chifukwa chopsa mtima. Nayonso mfumu yathu Edipa yayankhula mtima ukuwawa. Mapokoso amenewa satithandiza kupeza njira yothetsera mavutowa. 13