Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 17

Sewero la Mfumu Edipa mene mwanena. TERESI: Ndanena kuti munthu amene mukumufunafunayo sali kutali ayi, ndi inu nomwe! EDIPA: Kameneka ndi kachiwiri kunena bodza loyipali, lomwe likhoza kukulowetsani m’mavuto owopsa. TERESI: Mukufunanso ndikuwuzeni zambiri kuti mukwiye zenizeni? EDIPA: Mukhoza kuchita zimene mukufuna. TERESI: Ndikunenazi ndi zowona, kungoti inuyo simukudziwa. Moyo umene mukukhala ndi wochititsa manyazi kwambiri. N’zomvetsa chiso- ni kuti ngakhalenso banja lanu silikudziwa. EDIPA: Mukuganiza kuti munganyazitse mfumu n’kungosiyidwa ulele? TERESI: Ngati chowonadi chilidi champhamvu palibe chingandichiti- kire. EDIPA: Chowonadi chilidi ndi mphamvu, koma osati kwa anthu ama- bodza ngati inuyo. Inuyo mulibe chowonadi ngakhale kadontho chifu- kwa zonse, kuyambira makutu, maganizo komanso maso anu, ndi zaku- fa. Zinafa kalekale. TERESI: Komatu mukuchitaku ndi kusaganiza bwino, chifukwa mawu oyipa mukundinenerawa akutembenukirani. EDIPA: Sindikuwopa zimenezo. Ndi maso anu amdimawo simungakwa- nitse kulimbana nane. Ngakhale munthu amene amawona bwinobwino sangalimbane ndi ine. Ndiye kuli bwanji wopanda maso ngati inu! TERESI: Ndikunenazi ndi zowona ndithu. Ndipo musade ine chifukwa si ine amene ndachititsa kuti mukumane ndi tsoka limeneli. Muzimuyi- mba mlandu Apolo. EDIPA: Ayi musandinamize, Kireyo ndi amene wakutumani, n’zosathe- ka kuti mungoyamba kunena zimenezi poyerayera. TERESI: M’manja mwa Kireyo ndi moyera. Mavutowa munawapalamu- la nokha bambo. EDIPA: Anthu inu ndi oyipa kwabasi. Munthu asalemere ayi, asakhale mfumu kapena kukhala ndi luso linalake koma kumuchitira nsanje basi. 12