Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 16

Sewero la Mfumu Edipa TERESI: Ngakhale mukunena kuti ndine wodzikonda, dziwani kuti inuyo ndi amene mukulephera kuwona kudzikonda kumene muli nako. Koma n’zomveka, paja chala sichiloza mwini! EDIPA: Ndi munthu wamtundu wanji amene angapitirize kumvetsera zimenezi osapsa mtima. Musaganizetu kuti tidwala m’mimba chifukwa choti simunatiwuze zimene mwawona. TERESI: Inde simudwala. Komabe dziwani kuti chinsinsi chimenechi chikatumbuka chikubowolani m’mimba. EDIPA: Ndiye popeza mwati chitumbuka, ndiye bwanji osangonena? TERESI: Pepani kwambiri. Akuluakulu anati, ukayenda siya phazi, uka- siya mulomo umakutsata. EDIPA: Ndinu munthu wosathandiza ngakhale pang’ono, moti mwa- ngotitayitsa nthawi yathu yamtengo wapatali. Ndikutha kuwona kuti nanunso munatengapo mbali pachiwembuchi. Mwinanso n’chifukwa chake simukufuna kuyikapo mlomo. TERESI: Mwatero? Inutu mukungofuna kundiyankhulitsa pambali! Zi- kanakhala kuti ndinakonza nawo chiwembucho ndikanakuwuzani kuti mundiphe. Mwina ndikumasuleni tsopano, munthu amene akuchititsa kuti mzindawu uthimbirire mpaka milungu kukwiya ndi inuyo. EDIPA: N’chifukwa chiyani mukuyankhula zoduka mutu? Mukuganiza kuti mungayankhule mawu amenewa osalangidwa? Dikirani muwone. TERESI: Inetu sindilangidwa. Chowonadi n’chimene chinganditeteze. EDIPA: Ndi ndani wakuwuzani zimenezi? Sizingatheke kuti mungo- bwera pano n’kuyamba kundiloza chala. TERESI: Inuyo ndi amene mwandiwuza. Pajatu ine sindimafuna kuya- nkhula, koma mwachita kundikakamiza. EDIPA: Mukutanthawuza chiyani? TERESI: Muziyankhulatu chilungamo inu! Mukunenetsa kuti simuna- mve zomwe ndanena zija? Kapena mukungofuna kunditapa mkamwa? EDIPA: Sindikukuyesani. Ndafunsa chifukwa ndikufuna kumvetsa zi- 11