Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 15

Sewero la Mfumu Edipa adzazimitsa zako. TERESI: Mfumu yanga, inetu ndikusowa chonena! Kodi nzeru zinga- khale zaphindu lanji ngati zitamubweretsera munthu mavuto? Ndisaku- namizeni pano kuti sindimadziwa nkhaniyi. Ndimayidziwa ndithu, ku- ngoti ndinasankha kungoyiponya kunkhongo. Musaganize kuti ndika- nabwera kuno mukanapanda kutuma munthu kuti adzanditenge. EDIPA: Bwanjinso, pali vuto kapena? N’chifukwa chiyani nkhope yanu ikuwoneka yakugwa? TERESI: Ngati n’zotheka, chonde ndiloleni kuti ndibwerere kwathu. Ti- yeni tingokhutitsidwa ndi mavuto amene akuchitikawa m’malo moti ti- zitokosolanso ena aphe-e. EDIPA: Zimene mwanenazo si zolimbikitsa ngakhale pang’ono, koma- nso zikusonyeza kuti ndinu munthu wodzikonda kwambiri. TERESI: Nanunso zimene mwanenazo ndi zosalimbikitsa ngakhale pa- ng’ono. Inetu sindikufuna kuyikapo mlomo pa nkhaniyi chifukwa sindi- kufuna kuwonjezera mavuto alipo kalewa. EDIPA: Ngati mukudziwa pomwe pagona vuto, bwanji osangonena? Zo- wona mukufuna tichite kukunyambitani mapazi komanso kung’amba kukamwa kuti mutiwuze? TERESI: Inuyo mbuyanga mfumu ndinu munthu wosamva za ena. N’chifukwa chiyani mukundikakamiza kuti ndikuwululireni chinsinsi chowopsa ngati chimenechi, chomwenso chikhoza kukubweretserani mavuto aakulu? EDIPA: Mukutanthawuza chiyani? Mukufuna mundiwuze kuti simune- na chilichonse ngakhale mzindawu uwonongeke? TERESI: Ineyo sindikufuna kudzibweretsera mavuto kapena kukubwe- retserani chisoni. N’chifukwa chiyani mukuvutika ndi nkhani imeneyi? Palibetu chimene mutapindulepo. EDIPA: Ndinu munthu wotembereredwa kwambiri! Anthu ngati inu mukhoza kupsetsa mtima ngakhale mwala! Zowona mukukanika ku- ngotiwuza zimene mulungu wakuwululirani? Koma ya-a! Anthu enadi amakhala owuma mitima ngati mfiti. 10