Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 14

Sewero la Mfumu Edipa EDIPA: Usadandawule, ndachita kale zimenezo. Kireyo anandiwuzanso zomwezo moti ndatuma munthu kuti akamutenge. Ndikudabwa kuti n’chifukwa chiyani sakutulukira mpaka pano? MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Kuwonjezeranso pamenepo, pali mphekesera zinanso zokhudza nkhaniyi zomwe zinkamveka kalelo. EDIPA: Mphekesera zake zotani? Ndikufuna kumva chilichonse chokhu dza nkhani imeneyi. MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Zimamveka kuti mfumu Layasi inaphedwa ndi anthu apawulendo. EDIPA: Enanso anandiwuza zimenezo, koma palibe amene ananditsimi- kizira kuti ndi zowona. MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Koma ndikuganiza kuti ndi ma- temberero mwanena aja, munthu amene anachita zimenezi abwera poye- ra, chifukwa akapanda kutero adzibweretsera tsoka lowopsa. EDIPA: Komatu usayiwale kuti munthu akafika popha munthu mtima wake umakakala moti samawopanso chilichonse. MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Ndikudziwa, koma osati ngati pali munthu yemwe akhoza kumubweretsa poyera. A Teresi ndi awo akubwera apowo, mneneri wokhala ngati mulungu, yemwe amawona zinthu zosawoneka ndi maso. [Akulowa TERESI akutsogoleredwa ndi MNYAMATA.] EDIPA: Takulandirani a Teresi, mneneri wathu. Timadziwa kuti ndinu munthu wozindikira kwambiri. Mumadziwa zinthu zomwe palibe ame- ne angazimvetse. Mumadziwanso ngakhale zinthu zomwe zimachitika kumwamba. Ngakhele kuti ndinu wakhungu, ndikuganiza kuti muku- dziwa bwino kuti dziko lathuli lawoleratu. Choncho takuyitanani kuti mutithandize kumvetsa zimene Apolo wanena. Apolo akuti mliri wati- gwerawu ukhoza kutha ngati titapeza anthu amene anapha Mfumu La- yasi. Choncho tiwuzeni chimene mwawona kapena kumva kuchokera kwa milungu. Chonde pulumutsani mzindawu komanso dzipulumitse nokha potiwuza zolondola zokhudza nkhaniyi. Miyoyo yathu ili m’ma- nja mwanu tsopano. Paja amati mnzako akapsa ndevu m’zimitse, mawa 9