Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 13

Sewero la Mfumu Edipa wa ku Thebesi kuno ndi amene wandiwuza zimenezi ndipo n’kupusa kwambiri kuchita zosemphana ndi zimene mulungu wanena. Choncho ndikutemberera aliyense amene anapha Layasi kuti moyo wake usapeze mtendere ngakhale pang’ono. Ndikupempheranso kuti aliyense amene angalandire munthu wotero kunyumba kwake akumane ndi masoka onse amene munthu amene anapha mfumuyi angakumane nawo. Nga- khale zikanakhala kuti milungu sinatilamule kuchita zimenezi, timaye- nerabe kuzichita. Timayenera kubwezera imfa ya mfumu yathu yomwe inaphedwa yosalakwa. Ndiye popeza tsopano ndili ndi mphamvu zime- ne mfumuyo inali nazo komanso ndinalowa m’nyumba yake n’kumube- rekera ana, ndiwonetsetsa kuti chilungamo chachitika. Ndimenya nkho- ndo m’malo mwake. Ndichita zimenezi mofanana ndi zimene mwana amachita pobwezera anthu amene anapha bambo ake. Kwa amene saku- funa kutsatira zimene ndalamulazi, ndikupempha kuti milungu iwafula- tire, nthaka yawo ikhale yosabala, akazi awo akhale osabereka, komanso onse atikitidwe ndi mliri wagwawu. Koma nonse amene mutamvere zimene ndakuwuzanizi, mtendere ukhale nanu ndipo milungu ikukhu- thulireni madalitso. MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Mbuyanga mfumu, popeza the- mbereroli mwalilunjika kwa ine, ndikufuna ndikuwuzeni kuti ndinapha Layasi si ine, komanso ndingakutsimikizireni pano kuti sindikudziwa amene anamupha. Ngati mukufuna kudziwa amene anamupha munga- chite bwino kukafunsa Apolo yemweyo, chifukwa ndi amene watakasa nkhaniyi. Mwina angakakutchulireninso dzina lake. EDIPA: Zimene wanenazo ndi zowona. Komatu palibe munthu amene angakakamize mulungu kuti ayankhule asakufuna. MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Kodi mungalole kuti ndikupa- tseniko uphungu pang’ono? EDIPA: Usachite mantha, yankhula. MTSOGOLERI WAGULU LA ANTHU: Ine ndikudziwa kuti tili ndi mneneri wathu kuno, yemwe amatha kuwona zinthu mofanana ndi mu- lungu wathu Apolo. Bwanji osamufunsa ameneyo? Mwinatu akhoza kukuthandizani kudziwa amene anapanga chiwembuchi! 8