Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Sewero la Mfumu Edipa | Page 11

Sewero la Mfumu Edipa KIREYO: Onse anaphedwa, kupatulapo m’modzi. Munthuyo atafika kuno anafotokoza zonse zimene anawona. Koma pali chimodzi chimene sankafotokoza bwinobwino. EDIPA: N’chiyani chimene sanafotokoze bwinobwinocho? Mwina kudziwa zimenezo kungatithandize kuwona ulusi womwe tingatole kuti titsate nkhaniyi. Tikapanda kuchidziwa tikhoza kumangopupulika m’mabodza n’kupezeka kuti tayamba kuyenda tikufuka utsi. KIREYO: Anatiwuza kuti mfumuyo inaphedwa ndi achifwamba, osati munthu m’modzi, koma gulu la achifwamba. Ankati achifwambawo anawawukira mwamphamvu kwambiri moti zinali zosatheka kupulu- mutsa mfumuyo. EDIPA: Ndikuganiza kuti pali munthu winawake ku Thebesi kuno yemwe anawatuma kuti achite zamtopolazi. KIREYO: Ifenso tinkaganiza choncho. Koma Layasi atangophedwa, tina- kumananso ndi vuto lina lowopsa kwambiri lomwe linatiphimba m’ma- so n’kutilepheretsa kubwezera anthu okhetsa mwaziwo. EDIPA: Koma zowona zimenezo? Mukundiwuza kuti mfumu ya mzinda uno kuphedwa inu n’kuyiwala kulanga anthu oyipa omwe anayipha? Koma ndiye munalakwitsadi kwambiri! Ndi vuto lanji lomwe linafika pokupanikizani mpaka kuyiwala kulanga anthu omwe anachita chosalu- ngama chimenechi? KIREYO: Chinali chilombo chowopsa chija, chija chinkayimba nyimbo yosadziwika. Chilombocho n’chimene chinachititsa kuti tiyike nkhani yofunikayi pambali. Tisanameyi, miyoyo yathu inali pachiswe. EDIPA: Popeza zinachitika zinatha, ndiyesetsa kuchitanso zofanana ndi zimene ndinachita pa nthawi imene ija. Koma dziwani kuti n’zomveka kuti Apolo atilange chonchi chifukwa tinachita zinthu molekerera kwa- mbiri. Choncho ndigwira ntchito limodzi ndi mulungu wathuyu koma- nso inuyo, kuti tipeze anthu amene anapha mfumuyi. Ndikuyenera ku- chotsa chodetsa chimenechi msanga chifukwa n’kutheka kuti anthu ame- newo angakhale akulinganizanso zoti andisowetse ineyo. Choncho ngati nditabwezera imfa ya Mfumu Layasi, ndiye kuti ndadzipulumutsanso ndekha. Choncho nyamukani nonse mupite kukayitana anthu onse kuti 6