Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 41

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: Ukadzaona chipsolopsolo chikuyendayenda pamudzi winawake, ndiye kuti chaona kansoti. Chipumi bii: Mawu achipongwe onena za munthu yemwe simukufuna mutamuona. Chitsanzo: Kukadzakhala madyerero mudzamuona ali chipumi bii, kubwera kudzadya nawo. Chipumi: Mwana. Chitsanzo: Amanenetsa kuti safuna kudzamwalira asanasiye chipumi chawo padzikoli. Chipupa: (a) Khoma. Chitsanzo: Chipupa cha nyumba chinawagwera. (b) Munthu wosasunthika. Chitsanzo: Amene uja ndi chipupa, simungamuthe. Chipwirikiti: Chisokonezo. Chitsanzo: Apolisi anaphulitsa utsi wokhetsa misozi ndipo m’tauni monse munali chipwirikiti. Chirombo: Munthu wamphamvu kwambiri kapena munthu wankhanza mwinanso wouma kapena woipa mtima. Chitsanzo: Zimakhala zovuta kuti uzindikire kuti munthuyu ndi chilombo mukakhala pachibwenzi. Chisakasa: Chinthu chosamangidwa mwadongosolo kwenikweni. Chitsanzo: Amanga chisakasa chawo kumunda kuja. Chisembwere: Chiwerewere. Chitsanzo: Mayi opemphera aja anawagwira akuchita zachisembwere. 40