Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 329
Paphata pa Chichewa
Pita panzeru: Kuposa wina pa nzeru.
Chitsanzo: Anangochepa koma amakupitani panzeru.
Pita poduka mphepo: Kupita popanda anthu, paokha.
Chitsanzo: Tiyeni tikakumane poduka mphepo.
Pokoma anatayira galu: Munthu wopanda pabwino,
anthu akamuchitira zabwino iye amabweza zoipa.
Chitsanzo: Mwana wanuyu alibe pabwino, pokoma
anatayira galu.
Pokonyola khosi (potola khosi): Kupotokola khosi la
munthu.
Chitsanzo: Zikuoneka kuti anamupha atamupokonyola
khosi.
Pokopoko: Phokoso la anthu omwe akukangana.
Chitsanzo: Ndani angasangalale kuti pakhomo pake paz-
ingozi pokopoko!
Polaa: Kupolama.
Chitsanzo: Tikaphe mpola, mbalame zili polaa!
Polama:
(a) Ima mowerama.
Chitsanzo: Takaimani uko musalipolamire apa!
(b) Ena amanena mawuwa potanthauza kuti akukumana
ndi mavuto chifukwa cha Satana.
Chitsanzo: Chaka chino Satana watipolamira.
Ponda chitsononkho: Kulakwitsa chinachake.
Chitsanzo: Munthu wina akaponda chitsonokho
osamaseka, mawa ukhoza kudzakhala iwe.
Ponda lupsa: Kukula, kuyamba kusamba kapena
kutulutsa umuna.
Chitsanzo: Wayamba kuvuta mmene waponda lupsamu.
Ponda mabuleki: Ima kaye, siya kuchita zinthu zosa-
longosoka.
Chitsanzo: Nditaona kuti anthu ambiri akutenga
328