Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 328

Paphata pa Chichewa Pintchapintcha: Kupintchama, kulephera kuyenda bwinobwino. Chitsanzo: Akuyenda pintchapintcha chifukwa wabinya. Pinyolo: Kupereka chinthu chako kwa wina kuti akupatse ndalama kapena chinachake. Chitsanzo: Aponyoletsa njinga yawo. Piringupiringu: Kumangoyendayenda kwa anthu ochuluka. Chitsanzo: Mmene ndimafika n’kuti anthu ali piringupiringu. Pisa khoswe mu ufa: Kusiyira mbala zinthu zomwe akhoza kuziba. Chitsanzo: Kumusiyira munthu ameneyu pakhomo pano n’kupisa khoswe mu ufa. Pisa m’maso: Kupita kukaona munthu kapena chinthu, kuyendera munthu. Chitsanzo: (1) Anabwera kuti akupiseni m’maso. (2) Ndangoti ndidutseko kuti ndikupiseni m’maso. Pisa m’matumba: Kukuthera ndalama, kukutengera ndalama zonse. Chitsanzo: Mukapanda kusamala akupisani m’matumba. Pita kumanzere: Kukukanika, kusachita bwino zinazake. Chitsanzo: Masewera a mpira anandipita kumanzere. Pita kumwezi: Matenda a akazi omwe amadwala mwezi ndi mwezi, kusamba. Chitsanzo: Mkazi amayenera kuyala kampango pabedi akapita kumwezi. Pita padera (pita pachabe): Kubala mwana wakufa. Chitsanzo: Zimandimvetsa chisoni mayi kudikirira miyezi isanu ndi inayi n’kupita padera. Pita pansi (yenda pansi): Namiza. Chitsanzo: Apa ndiye mwandipita pansi (mwandiyenda pansi), mugulitsa bwanji mbuzi osandiuza? 327