Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 181

Paphata pa Chichewa Kupita kumanzere: Kusagwirizana nacho, kusakwanitsa kuchita chinthu. Chitsanzo: (1) Nyemba zinandipita kumanzere. (2) Masewera a mpira anandipita kumanzere. Kupita m’madzi (kulowa m’madzi): Kupita pachabe, kungoonongeka. Chitsanzo: Ndalama yanga yangolowa m’madzi. Kupita mphepo: (a) Kuzizira. Chitsanzo: Chisiyeni chakudyachi chipite kaye mphepo. (b) Kukhala kaye osadya. Chitsanzo: Mwana iwe pakamwa pako padzipita mphepo! Kupita pachabe: (a) Kubereka mwana wakufa, kuchoka kwa mimba nthawi yake isanakwane. Chitsanzo: Mayiwa ali ndi vuto, akatu ndi kachitatu kupi- ta pachabe. (b) Kusagwira ntchito yake yoyenerera. Chitsanzo: Khama langa langopita pachabe. Kupita pansi: Kuchitira wina chiwembu, kupusitsa munthu. Chitsanzo: (1) Anthu a m’mudzi uno ayamba kundipita pansi, ndiyenera kumakhala wosamala. (2) Atambwali okhaokha sangapitane pansi. Kupitana n’kupitana: Kuchitirana chipongwe, kutukwanizana. Chitsanzo: Anthu amenewa amapitana n’kupitana. Kupitidwa mphepo ina: Kukaonako zina. Chitsanzo: Ndipite kumudzi kuti ndikapitidwe mphepo ina. Kupola: (a) Kuchira. Chitsanzo: Bala langa silinapole. 180