Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 75

Miyambi ya Patsokwe Zinthu zina zimachitika mwadzidzidzi chifukwa cha zinazake, ndipo pambuyo pake zimadziwika. Kalowa m’bwalo, sikatuluka. -Zinthu zosangalatsa zimavuta kuzisiya. Kalowa m’khutu kayala mphasa. -Chomwe munthu wamva chimakhazikika. Kalulu anamva mawu oyamba. -Mawu oyamba ndi amene amakhala aphindu komanso ndi amene anthu amagwira. Tizichenjera tikamanena zinthu chifu- kwa anthu amagwira mawu anthu oyamba. Kalulu anatuma njovu. -Mwambiwu utanthauza pamene munthu wolemekezeka aku- chita zinthu zina atatumidwa kapena m’malo mwa anthu ena onyozeka. Kamakuwa ndi kakumsampha, kam’diwa sikayankhula. -Wina akagwidwa ndi ndalama yobedwa, sayankhula. N’zachi- dziwikire kuti ndi amene anatenga ndipo amugwira basi. Kamanenepetsa sikadziwika. -Ndi bwino kumayesa njira zosiyanasiyana monga kulima ko- manso kugwira ntchito. Osamangodalira chimodzi. Kamanga zula. -Ndi bwino kumathetsa zimene zikuyambitsa mavuto ako, vuto- lo lisanakule. Kamapikula nkhali ndi katsekera. -Mwambiwu umanena za munthu amene amakonda kuchepetsa zinthu, pomwe zotsatitira zake ndi zazikulu. Kamata m’kati, ng’oma ya chimbulimbuli. -Mawuwa amanena mokokomeza za munthu amene amaoneka ngati wabwino pamaso koma mumtima mwake muli chiwembu. 74