Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 74

Miyambi ya Patsokwe amavutika kwambiri. Palibe munthu amene angathe kuchita zonse payekha, choncho ndi bwino kumadalirana. Kalikonse kamakhala ndi chiyambi. -Palibe chimene sichikhala ndi poyambira. Kalikonse kouluka kamatera. -Tingatchuke kapena kulemera bwanji, tsiku limadzafika loti ti- madzasauka kapena kudzamwalira n’kusiyana nazo zonse. Moyo umanyenga. Kalindelinde adalinda chiswe. -Mlesi amataya mwayi wogwira ngumbi pamene zituluka. Pope- za wachedwa kudzuka, amapeza zatha ndipo amangopeza chiswe. Kalionera adaphika ntchentche kuyesa ana a Njuchi. -Munthu ukamatengera makhalidwe oipa a anthu, amene uma- kumana ndi mavuto ndi iweyo. Osamatengera zoipa zomwe ena amachita. Kalira-ulendo salira, ndi mtu uchepa. -Munthu akamapita kwinakwake kukafuna zinthu monga zovala kapena zakudya, amayenera kutenga zimene angapeze. Akhoza kubwerera opanda kalikonse ngati atamaderera n’ku- masiya zinthu. Kalongoda sapsera madzi amodzi. -Zinthu zina zimafunika khama kuti zitheke. Komanso kuti munthu achite bwino amafunika kuthandizidwa kangapo. Kalowa m’bwalo kali ndi nyimbo. -Munthu akayamba kuchita zinazake ndiye kuti pali chimene chikumulimbitsa mtima. Kalowa m’bwalo kayanza malo. -Zimakhala zovuta kuimitsa chinthu chimene chayamba kale. 73