Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 29

Miyambi ya Patsokwe kuchenjera pakakhala palibe mavuto, koma mavuto akagwa amafuna kuti anthu ena amuthandize. Chenjerechenjere sadzimeta, amakumeta ndi mnzako. -Ngakhale munthu aoneke wochenjera motani, monga kuthawa ntchito za gulu ngati pamaliro, tsiku lina zimadzamugwera ndipo amadzafuna chithandizo cha ena. Chenjerechenjere samapha nsomba, amapha nsomba n’kombe. -Kuyankhula kwambiri pantchito sikusonyeza kuchenjera. Siku- tanthauza kuti ntchito ikugwiridwa, koma kugwira ntchito n’ku- mene kumayendetsa ndime. Chenjerechenjere, anapsa ndi phala logona. -Kusamva kapena kuchenjeretsa kumabweretsa mavuto aakulu. Chete n’kunena (kukhala chete n’kunena). -Pa mlandu munthu akafunsidwa koma osayankha, ndiye kuti akuvomera kulakwa kwake. Chetechete ndi upumbwa, akoma ndi suyosuyo. -Tisamazengereze pogwira ntchito, koma kungogwiriratu pope- za zamawa sizidziwika. Chetechete sautsa nyama, autsa nyama n’kuwani. -Ngati munthu wakasuma kukhoti, uyeneranso kulongosola tsa- tanetsatane wa nkhani. Ngati sutero, mlanduwo ukhoza ku- kuvuta. Chetechete sautsa nyama, autsa nyama ndi suyo suyo. -Kungokhala chete sikuthandiza ngati munthu ukufuna kukwa- niritsa chinachake. Chetechete sautsa nyama, koma suyosuyo. -Kungokhala pamene mukuona zinthu zikulakwika sikuthandi- za, koma kuyankhula kuti zinthu zikonzedwe. 28