Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 28
Miyambi ya Patsokwe
Chapitamo wosenda luzi pamwala.
-Mawuwa amanena za munthu wodziwa kwambiri mankhwala
a zitsamba kuposa onse.
Chati chubwi! chisati kapa! sichinaoloke.
-Mawuwa amatanthauza kuti mawu oyamba ndi malonje chabe,
nkhani yeniyeni sinayambe.
Chati chubwi, sichinaoloke, koma chati kapakapa.
-Mawuwa amatanthauza kuti mawu oyamba ndi malonje chabe,
nkhani yeniyeni sinayambe.
Chati deru chadabwitsa mlenje.
-Kanthu sikachitika popanda chifukwa kapena choyambitsa
chake. Ndiye kachizindikiro kangachepe bwanji, tizikhala nako
tcheru.
Chati deru chawopsa mlenje.
-Munthu akasiya chizolowezi chake ndiye kuti chilipo chimene
chamudabwitsa kapena chamuchititsa mantha.
Chati khocho (tswa) sichinapite.
-China chake chikakudabwitsa, khala tcheru.
Chatuluka m’dzira n’chiyani?
-Mwamuna akamakana kuti si amene anachimwitsa mkazi, an-
thu amanena mawu amenewa pofuna kudziwa ngati mwana
wobadwayo akufanana ndi mwamunayo. Pa mlandu uliwonse
payenera kukhala umboni.
Chauluka chidzatera.
-Tingatchuke kapena kulemera bwanji, tsiku limadzafika loti ti-
madzasauka kapena kudzamwalira n’kusiyana nazo zonse.
Moyo umanyenga.
Chenjerechenjere pa m’meto, pa maliro panalibe.
-Mawuwa amanena za munthu amene amajijirika kapena
27