Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 27

Miyambi ya Patsokwe Chaomba guta. -Tsoka likagwera mlendo, anthu sadandaula kwenikweni. Koma chisoni chimakula pamene wapamudzi pomwepo wakumana ndi mavuto. Chaona maso, mtima suiwala. -Ndi bwino kumasamala ndi zimene timaona chifukwa zikhoza kutigwetsera m’mavuto aakulu monga chigololo. Zimene mun- thu waona amazikumbukira ngakhale patadutsa nthawi yaitali. Chaona mchira gondwa ali m’mphako. -Kusaonetsetsa kapena kusamvetsa zinthu kumapangitsa kuti munthu azinena nkhani popanda umboni weniweni. Chaona mnzako chapita, mawa chili pa iwe. -Osamasangalala ena akamakumana ndi mavuto chifukwa na- wenso akhoza kukupeza. Chaona munda wakuthungo, mawa chidzaona munda wapaka- ti. -Munthu ukakhala pabwino umaona ngati sungadzavutike. Nthawi zina munthu umatha kukumana ndi chinthu chimene sumayembekezera kuti chingachitike. Chaona mwana tola, ukulu n’kuona kako. -Chaona mwana chitole chifukwa udzadya naye. Tisanyozere chimene munthu amene ali pansi pathu wapeza, chifukwa chikhoza kutithandiza. Chaphulika chapsa, mkamwini konza nguwo. -Chinthu chikachitika, monga imfa, pamafunika kulimba mtima chifukwa chachitika chatha. Palibenso njira ina yochithetsera. Chapita apa wachiona ndi munthu. -Pa moyo wa munthu anthu ena ndi ofunika chifukwa amaku- chenjeza. 26