Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 30

Miyambi ya Patsokwe Chibale cha nkhondo, amawo akafa n’kumva ndiika nawo. -Mawuwa amanena za munthu amene si m’bale wako weniweni, koma chifukwa choti makolo anakhalira limodzi nthawi yaitali, amakhala ngati m’bale wako weniweni. Chibale n’chipsela. -Chibale sichitha. Chibale n’chipsera, sichitha. -Sitingathe kuthetsa ubale, zivute zitani. Chibale n’kuyenderana. -Kuti chibale chilimbe pamafunika kuyenderana komanso kuthandizana. Chibale ndi fupa, sichiwola. -Pangakhalitse abale osaonana, sikuti chibale chimatha. Chibale ndi fupa. -Chibale sichitha. Chibale ndi litsiro, sichisansika. -Chibale sichitha, abale amatha kuoneka ngati adana koma amadzagwirizana. Chibale pamowa. -Anthu amene amakhala mabwenzi zikamayenda, koma pa- mavuto amakuthawa. Chibangiri chimapita ndi mwini dzanja. -Sungakakamize munthu kuchita zimene sakufuna. Chibwana chidatayitsa nguwo ya njuzi. -Chifukwa cha chibwana, anthu amataya mwayi mwina wa ban- ja kapena ntchito. Chibwana n’chilonda, sichiona pokhala. -Anthu achibwana amakhala paliponse ndipo zochita zawo 29