Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 237

Miyambi ya Patsokwe Ukayenda siya phazi, ukasiya mlomo udzakutsata. -Tikayenda tizisiya mbiri yabwino osati kuchoka titasokoneza. Tisamanene mabodza. Ukayendera nzengo usamati Asakhwi afumbula. -Ukapita kukadula mitengo usaiwalenso chomwe wapitira n’kuyamba kuyang’ana Asakhwi. Anthu amanena mwambiwu ngati munthu amene watumidwa anayamba kuchita zina zosi- yana ndi zimene anamuuza. Ukapita kwinakwake, usamayambe kuchita zinthu zomwe sizinali cholinga chako. Ukayipa nkhope, dziwa nyimbo. -Ukazindikira kuti ndiwe wolephera pa chinachake, phunzira kuchita chinthu china. Ukaziputa limba. -Osamayamba dala mavuto ngati ulibe podalira. Ukaziputa, limba nazo. -Ukamapalamula kapena kuyamba mavuto monga banja uma- yenera kukhala utakonzeka kukumana ndi mavuto. Uko kulire n’kumtsukwa. -Mawuwa akutanthauza kuti kumene kukulira ndi kosongoka kwa khasu. Pamene pali nkhani yeniyeni ndi pamene pama- zunguza kwambiri. Ukonde umayambira ku wakale. -Poluka ukonde umangera ku wakale. Zinthu zatsopano zima- yambira ku zakale. Ukonzi unapha msemang’oma. -Chisoni nthawi zina chimapezetsa mavuto kuchokera kwa an- thu osayamika. Uku kwawinda, tikudya mawa mande. -Mawuwa amatanthauza kuti pali mapokoso kapena 236