Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 236

Miyambi ya Patsokwe zimene munthu uja anakatenga ndi zimene zinam’phetsa. Ukatambatamba uziyang’ana kum’mawa, kunja kungaku- chere. -Tikamachita zoipa monga kuba, chiwerewere tizizindikira kuti akadzangotigwira tidzakumana ndi mavuto. Mwambiwu umanena za kutamba chifukwa ena makolo akalelo ankakhulupirira kuti afiti amatamba usiku. Ukatchula Mkango, kwera m’mwamba. -Ukamanena za munthu wina ndiye kuti ali pafupi. Mawuwa amanenedwa ndi ena ngati njira yokupulumutsira kuti mun- thuyo asakumve ukumunena. Anthu akamanena za munthu wina, nthawi zambiri amakhala ali pafupi. Ukatukwana ng’ona, kumadzi usapiteko. -Ngati tapalamula timasowa mtendere mumtima podziwa kuti chilango chikutidikira. Ukayenda m’fumbi usadane n’kutuwa. -Sitingathe kulekanitsa zinthu zoyendera limodzi monga fumbi ndi kutuwa. Kumavomereza zinthu zina zikachitika. Ukayenda m’tchire (m’thengo) wayendera zonse. -Nthawi zina ukamayendera zina umathanso kuchita mwayi wochitanso zina. Pamene munthu akupita kwinakwake kukatenga chinthu, kumeneko amatha kukapezanso china chomwe sanachiganizire ndipo ayeneranso kuchitenga. Ukayenda ndi mwana wayenda wekha. -Osamadalira kwambiri ana ukamachita zinthu. Ukayenda panjira usamagulule mano, udzasowa chodyera nyama. -Tisanayambe kuchita chinthu tiziona kaye kuti tili ndi zonse zo- funikira. 235