Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 238

Miyambi ya Patsokwe chisokonezo ndiye anthu adya bwinobwino mawa zimenezi zikatha. Ukamachita phwando ndi bwino kukonzekera chifu- kwa anthu amawerengera kuti adzadya. Ena amachita kukhwe- fula malamba awo kuti adzadye zambiri. Ukufunsa za phula, njuchi ndi izi ukuziona. -Mawuwa amanena za munthu amene akufunsa zinthu zoti aku- zidziwa kale. Ukukonda bwemba osakonda chulu! -Usakonde bwemba koma chulu pamene pamera bwembayo. Mawuwa amanena za mwamuna yemwe amakonda mkazi wake yekha koma osati apongozi ake. Ukulu si msinkhu ayi. -Kutalika kapena kubadwa kale si nzeru koma kuchita kapena kuyankhula zakupsa. Ukundisokosera n’kulinga utamva. -Mfundo za mawu timazipeza tikamvetsera kaye. Ulemu n’kubadwa nawo. -Tiyambiretu kuphunzitsa ana athu makhalidwe abwino adakali aang’ono. Ulemu n’kuthirana. -Ukachitira wina ulemu nayenso amakupatsa ulemu. Ulemu ndi mpira, umabwerera. -Mawuwa amayerekezera ulemu ndi mpira womwe ukaulandira umafunika kupatsira wina. Tizichitira ena ulemu, tikapanda ku- wapatsa ulemu nawonso satipatsira mpira. Ulemu wa Buluzi m’nyumba ya mfumu. -Anthu ena amalandira ulemu chifukwa cha makolo komanso anthu amene akukhala nawo, pomwe iwowo ndi onyozeka. 237